LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 2 tsa. 5
  • Kukambilana Mwacibadwa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kukambilana Mwacibadwa
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Kukamba Mwaumoyo
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kukamba Motsimikiza
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Mzimu Waubwenzi na Cifundo
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 2 tsa. 5

PHUNZILO 2

Kukambilana Mwacibadwa

Lemba losagwila mawu

2 Akorinto 2:17

ZOFUNIKILA: Muzikamba mwacibadwa ndiponso moona mtima, poonetsa mmene nkhaniyo imakukhudzilani imwe komanso omvela anu.

MOCITILA:

  • Mwa pemphelo, konzekelani bwino. Pemphelani kuti Mulungu akuthandizeni kuika maganizo anu pa uthenga wanu, osati pa inu mwini. Sumikani maganizo anu pa mfundo zazikulu zimene mufuna kuzimveketsa. Fotokozani mfundozo m’mawu anu-anu; osati kukamba mawuwo ndendende mmene awalembela iyai.

    Tumalangizo tothandizila

    Ngati mufuna kukaŵelenga Baibo kapena cofalitsa cina, konzekelani bwino kuti mukaŵelenge bwino-bwino, osati molumila-lumila. Ngati muŵelenga mawu ogwidwa a munthu wina, ŵelengani na mzimu wake, koma osati mopambanitsa.

  • Kukamba mocokela pa mtima. Ganizilani cifukwa cake kuli kofunika kuti omvela anu amve nkhani yanu. Lunjikitsani maganizo anu pa iwo. Mukatelo, kaimidwe kanu, magesca, nkhope yanu, zonse zidzaonetsa kuona mtima kwanu, komanso mzimu waubwenzi.

    Tumalangizo tothandizila

    Kukamba mwacibadwa sikutanthauza kukamba mosasamala. Sungani ulemu wa uthenga wanu mwa kulankhula momveka bwino, komanso kukamba Cinyanja cabwino.

  • Yang’anani omvela anu. Muziyang’ana omvela anu pokamba nawo. Pokamba nkhani, muziti mwayang’anako uyu, mwapita pa wina, basi telo, m’malo mongomwaza maso cisawawa pamwamba pa mitu ya omvela anu.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2022)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2022 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani