LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 5 tsa. 8
  • Kuŵelenga Bwino

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuŵelenga Bwino
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 5 tsa. 8

PHUNZILO 5

Kuŵelenga Bwino

Lemba losagwila mawu

1 Timoteyo 4:13

ZOFUNIKILA: Ŵelengani mokweza mawu, komanso ndendende mmene awalembela.

MOCITILA:

  • Konzekelani bwino. Dziŵani cifukwa cimene analembela nkhaniyo. Yesezani kuŵelenga magulu a mawu, osati liwu limodzi-limodzi. Samalani kuti musaikilepo mawu, kulumphila, kapena kuchula mawu ena ofananako. Samalani zizindikilo zonse za m’kalembedwe.

    Tumalangizo tothandizila

    Pemphani mnzanu kuti azitsatila pamene muŵelenga, ndipo azikuchulilani mawu alionse amene mwalakwitsa.

  • Chulani liwu lililonse moyenelela. Ngati simudziŵa mochulila bwino liwu, iyang’aneni mu dikishonale, kapena imvetseleni pa lekoding’i ya cofalitsa, kapena funsilani kwa munthu amene amaŵelenga bwino.

  • Muzikamba momveka bwino. Muzichula mawu mowamveketsa bwino, mutaŵelamutsa mutu wanu na kutsegula bwino pakamwa panu. Yesetsani kumawachula bwino-bwino mawu.

    Tumalangizo tothandizila

    Koma musacite kunyanya nako kachulidwe kabwino ka mawu, cakuti n’kucoka pa cibadwa.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2022)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2022 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani