LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 6 tsa. 9
  • Kumveketsa Bwino Cifukwa Coŵelengela Lemba

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kumveketsa Bwino Cifukwa Coŵelengela Lemba
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Kachulidwe ka Malemba Koyenela
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Mawu Otsiliza Ogwila Mtima
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kumveketsa Phindu ya Nkhani
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 6 tsa. 9

PHUNZILO 6

Kumveketsa Bwino Cifukwa Coŵelengela Lemba

Lemba losagwila mawu

Yohane 10:33-36

ZOFUNIKILA: Osangoŵelenga lemba basi n’kupita pa mfundo yotsatila iyai. Onetsetsani kuti omvela anu akuona bwino-bwino kugwilizana kwa lemba imene mwaŵelenga na mfundo imene mukufotokoza.

MOCITILA:

  • Onetsani mawu ofunikila. Mukaŵelenga lemba, onetsani mawu okhudzana na mfundo yanu yaikulu. Mungacite zimenezi mwa kuwabweleza mawu amenewo, kapena kufunsapo funso lopangitsa omvela anu kuwachula mawu ofunikilawo.

    Tumalangizo tothandizila

    Ngati muchula mawu osiyana-siyana pofuna kumveketsa mfundo ya lembalo, onetsetsani kuti omvela anu akuonabe bwino-bwino kuti mawu a m’Baibo amenewo akugwilizana na mfundo yanu yaikulu.

  • Gogomezani mfundo yanu. Ngati poŵelenga lemba mwamveketsa bwino cifukwa coliŵelengela, fotokozani mmene mawu ofunikila a pa lembalo amaonetsela cifukwaco.

    Tumalangizo tothandizila

    Pokambilana lembalo, Baibo yanu ikhale yotsegula. Izi zimathandiza omvela anu kugwilizanitsa zimene mukamba na lemba limene mwaŵelenga.

  • Mveketsani mosavuta colinga ca lembalo. Pewani kufotokozapo mfundo zina zosathandiza kweni-kweni kumveketsa mfundo yaikulu. Malinga na zimene omvela anu akudziŵa kale pa nkhaniyo, onani kuti ni mfundo zingati zimene mungafunike kufotokoza kuti mumveketse mfundo yanu.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2022)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2022 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani