LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 19 tsa. 22
  • Yesetsani Kuwafika pa Mtima Omvela

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Yesetsani Kuwafika pa Mtima Omvela
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Kukamba Mwaumoyo
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kumveketsa Phindu ya Nkhani
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Khalani Wolimbikitsa Komanso Wotsitsimula
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 19 tsa. 22

PHUNZILO 19

Yesetsani Kuwafika pa Mtima Omvela

Lemba losagwila mau

Miyambo 3:1

ZOFUNIKILA: Thandizani omvela anu kuona kufunika kwa zimene akuphunzila kuti acitepo kanthu.

MOCITILA:

  • Thandizani omvela anu kudziunika. Funsani mafunso othandiza omvela anu kuunikanso maganizo awo.

  • Kambani mowalimbikitsa. Athandizeni kuganizila cifukwa cacikulu cocitila zinthu zabwino. Alimbikitseni kukhala na zolinga zabwino, monga kukonda Yehova, anthu anzawo, na ziphunzitso za m’Baibo. Kambilanani nawo omvela anu; osakamba mowalamula. M’malo mowacotsela ulemu, onetsetsani kuti atsala olimbikitsika, komanso ofunitsitsa kucitapo kanthu.

  • Apangitseni kumaonapo Yehova. Unikani mmene ziphunzitso za m’Baibo, mfundo zake, na malamulo opezekamo, zimaonetsela makhalidwe a Mulungu na cikondi cake pa ife. Limbikitsani omvela anu kukhala na mtima wofuna kudziŵa maganizo a Yehova kuti azicita zom’kondweletsa.

    Tumalangizo tothandizila

    Kumbukilani kuti Yehova ndiye amakoka anthu. Gwilitsilani nchito Mawu ake kulimbikitsila omvela anu.

MU ULALIKI

Ngati n’kotheka, funsani mafunso okuthandizani kudziŵa zimene womvela wanu amakhulupilila. Onani nkhope yake na kamvekedwe ka mawu ake kuti mudziŵe zimene akuganiza. Komabe, khalani woleza mtima. Womvela wanu afunika kuti afike pokudalilani coyamba, kuti amasuke na kukuuzani maganizo ake eni-eni.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2022)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2022 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani