Lachisanu, August 28
Mumatambasula dzanja lanu nʼkukwaniritsa zolakalaka za chamoyo chilichonse.—Sal. 145:16.
Mofanana ndi Yehova, ifenso tingapatse ena zinthu chifukwa chowakonda. Mwachitsanzo, kodi mukudziwa Mkhristu wina yemwe akufunika chakudya kapena zovala? Yehova angagwiritse ntchito inuyo kuti mumuthandize kupeza zimene akufunikira. Anthu a Yehova amadziwika kuti amathandizana pakagwa mavuto. Mwachitsanzo, pa nthawi ya mliri wa COVID-19, abale ndi alongo ankapereka chakudya, zovala komanso zinthu zina kwa anthu amene akuvutika. Ndipo ambiri ankapereka ndalama zothandiza pa ntchito ya padziko lonse. Izi zinathandiza kuti gulu lizipereka chithandizo padziko lonse. Abale ndi alongo anachita mogwirizana ndi lemba la Aheberi 13:16, lomwe limati: “Musaiwale kuchita zabwino ndi kugawira ena zomwe muli nazo, chifukwa Mulungu amasangalala ndi nsembe zoterozo.” w24.09 39:6-7
Loweruka, August 29
Muzitha kusankha zinthu zimene ndi zofunikadi kwambiri.—Afil. 1:10.
Taganizirani chitsanzo ichi. Mukufufuza ntchito yomwe ingakuthandizeni kuti muzisamalira banja lanu. Ndiye papezeka ntchito ziwiri. Mukuganizira mfundo zonse monga mtundu wa ntchitoyo, nthawi yomwe muziigwira komanso mtunda umene mungamayende ndi zina. Ntchito zonsezo ndi zoti Mkhristu angagwire. Komabe inuyo mukukonda ntchito imodzi chifukwa cha mtundu wake komanso malipiro ake. Ngakhale zili choncho, pali mfundo zinanso zimene muyenera kuziganizira musanasankhe zochita. Mwachitsanzo, kodi ntchitoyo iziwombana ndi nthawi yanu ya kumisonkhano? Kodi izikutherani nthawi yomwe mumafunikira kucheza ndi banja lanu ndiponso kulithandiza kuti likhale pa ubwenzi wabwino ndi Yehova? Kuganizira mafunso amenewa kungakuthandizeni kudziwa kuti “zinthu zimene ndi zofunikadi kwambiri,” ndi zokhudza kulambira kwanu komanso kusamalira banja lanu kuposa kupeza ndalama zambiri. Mukatero mungasankhe zochita zimene zingachititse kuti Yehova akudalitseni. w25.01 3:11-13
Lamlungu, August 30
Yehova ali pafupi ndi anthu a mtima wosweka.—Sal. 34:18.
Ngakhale ena akuchitireni zopanda chilungamo, musamakayikire kuti Yehova amakukondani komanso amakuonani kuti ndinu wamtengo wapatali. Ngati ‘mukudzimvera chisoni mumtima’ muzikumbukira kuti Yehova anaona zabwino mumtima mwanu ndipo anakukokerani kwa iye. (Yoh. 6:44) Nthawi zonse iye ndi wokonzeka kukuthandizani chifukwa amakukondani kwambiri. Chitsanzo cha Yesu chingatithandize kudziwa mmene Yehova amamvera. Ali padziko lapansi, Yesu ankakomera mtima komanso kuchitira chifundo anthu omwe ankaonedwa ngati osafunika. (Mat. 9:9-12) Mwachitsanzo, mayi wina yemwe ankadwala matenda aakulu atagwira chovala chake pokhulupirira kuti achira, Yesu anamulimbikitsa komanso kumuyamikira chifukwa cha chikhulupiriro chake. (Maliko 5:25-34) Yesu anatengera makhalidwe a Atate wake. (Yoh. 14:9) Choncho musamakayikire kuti Yehova amakuonani kuti ndinu wamtengo wapatali ndiponso amaona makhalidwe anu abwino, kuphatikizapo chikhulupiriro ndi chikondi chanu kwa iye. w24.10 40:4-5