Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (2005-2019)
Tulukani
Lowani
Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
Chilengezo
Chinenero chatsopano chomwe chilipo: Madagascar Sign Language

Lamlungu, September 8

Inuyo ndi mbadwa zanu musankhe moyo kuti mukhalebe ndi moyo.​—Deut. 30:19.

Kungouza ana anu kuti izi n’zoyenera izi n’zolakwika si kokwanira. Ndi bwino kuwathandiza kuganizira mafunso monga akuti: ‘N’chifukwa chiyani Baibulo limatsutsa zinthu zimene thupi lathu limalakalaka? N’chiyani chikunditsimikizira kuti kutsatira mfundo za m’Malemba kungandithandize kuti zinthu zizindiyendera bwino?’ (Yes. 48:17, 18) Mwana amene akufuna kubatizidwa ayenera kuthandizidwa kuti aganizire bwino zinthu zina. Ayenera kuganizira udindo umene munthu amakhala nawo akabatizidwa. Ayeneranso kuona zinthu zabwino zimene angapeze komanso mavuto amene angakumane nawo. Ndiyeno ayenera kuyerekezera zinthu ziwirizi n’cholinga choti aone kuti ubwinowo ndi waukulu kwambiri kuposa mavuto amene angakumane nawo. (Maliko 10:29, 30) Kuganizira mfundo zimenezi munthu asanabatizidwe n’kofunika chifukwa chakuti n’zimene zingamuthandize akadzabatizidwa. Mwana akathandizidwa kuganizira mfundozi akhoza kukhutira ndi zimene amakhulupirira. Iye sangakayikire kuti mfundo za m’Baibulo n’zothandiza nthawi zonse. w17.12 21-22 ¶14-15

Lolemba, September 9

Amaziitana potchula iliyonse dzina lake.—Yes. 40:26.

Ena mwa abale ndi alongo athu akuvutika ndi matenda aakulu. Ena ndi achikulire koma akusamaliranso achibale awo okalamba. Ena amavutika kwambiri kuti apeze zinthu zofunika pa moyo. Ndipo ena ali ndi mavuto ngati amene tatchulawa, osati limodzi koma angapo. Ngati Yehova amachita chidwi ndi zinthu zopanda moyo zimene analenga, kuli bwanji inuyo? Mumamutumikira chifukwa choti mumamukonda, osati chifukwa chakuti munalengedwa m’njira yoti muzingochita zimenezo. (Sal. 19:1, 3, 14) Atate wathu wakumwamba amadziwa chilichonse chokhudza ifeyo. Paja Baibulo limanena kuti ngakhale ‘tsitsi lenilenilo la m’mutu mwathu amaliwerenga.’ (Mat. 10:30) Wolemba masalimo amatitsimikiziranso kuti: “Yehova amadziwa za moyo wa anthu osalakwa.” (Sal. 37:18) Iye amaona mavuto amene tikukumana nawo ndipo amatha kutipatsa mphamvu kuti tipirire. w18.01 7 ¶1; 8 ¶4

Lachiwiri, September 10

Tabita, dzuka!​—Mac. 9:40.

Petulo ataukitsa Tabita, anthu anadabwa kwambiri moti ambiri “anakhala okhulupirira mwa Ambuye.” Zimenezi zinawalimbikitsa kuti azilalikira za Yesu komanso kuuza anthu kuti Mulungu ali ndi mphamvu youkitsa akufa. (Mac. 9:36-42) Mu nthawi ya Paulo anthu ena anaonanso munthu akuukitsidwa. Tsiku lina, mtumwi Paulo anali pamsonkhano umene unkachitika m’chipinda cham’mwamba ku Torowa, komwe panopa ndi kumpoto chakumadzulo kwa dziko la Turkey. Paulo anakamba nkhani mpaka pakati pa usiku ndipo mnyamata wina dzina lake Utiko ankamvetsera atakhala pafupi ndi windo m’chipinda chachitatu m’mwamba. Kenako iye anayamba kugona ndipo anagwa kuchoka pawindopo kufika pansi. N’kutheka kuti Luka, yemwe anali dokotala, ndi amene anayamba kufika pamene mnyamatayo anagwera ndipo atamuona ananena kuti sikuti wangokomoka koma wafa. Zitatero, Paulo anatsika masitepe n’kukumbatira thupi la mnyamatayo kenako n’kunena kuti: “Ali moyo tsopano.” Zimenezi ziyenera kuti zinadabwitsa anthu. Iwo ataona kuti mnyamata amene anafayo wauka “anatonthozedwa kwambiri.”​—Mac. 20:7-12. w17.12 5 ¶10-11

Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2019 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani