Citatu, May 31
Ika mtima wako pa magulu a ziweto zako.—Miy. 27:23.
Mfundo ya pa Yakobo 1:19, imagwila nchito kwa awo amene amapeleka uphungu. Yakobo analemba kuti: “Munthu aliyense akhale wofulumila kumva, wodekha polankhula, wosafulumila kukwiya.” Mwina mkulu angaganize kuti akudziŵa mikhalidwe yonse ya munthu amene akufuna kupatsa uphungu, koma kodi iye adziŵadi zonse? Miyambo 18:13 imatikumbutsa kuti: “Munthu aliyense woyankhila nkhani asanaimvetsetse n’ngopusa, ndipo amacita manyazi.” Conco, ni bwino kufunsa mwiniwake kuti afotokoze zoona zake. Izi ziphatikizapo kumvetsela coyamba musanalankhule. Mkulu angafunse kuti: “Kodi zinthu zili motani pa umoyo wanu?” “Kodi pali mbali imene tingathandizilepo?” Akulu akamamvetsela coyamba kwa abale na alongo awo kuti adziŵe zimene akupitamo, adzipeleka thandizo lofunikila komanso cilimbikitso. Kupeleka uphungu wothandiza sikungoŵelenga cabe malemba angapo kapena kupelekapo malingalilo ayi. Abale na alongo athu ayenela kuona kuti timawadela nkhawa, timawamvetsetsa, komanso tifuna kuwathandiza. w22.02 17 ¶14-15
Cinayi, June 1
Panafika mkazi wamasiye wosauka ndipo anaponyamo timakobidi tiŵili tating’ono.—Maliko 12:42.
Umoyo ni wovuta kwambili kwa mkazi wa masiye. Ndipo cioneka kuti zimamuvuta kupeza zofunikila pa umoyo. Ngakhale n’telo, iye akupita pa kabokosi koponyamo zopeleka. Ndipo mosadzionetsela aponyamo tumakoboli tocepa kwambili tuŵili, tumene mwina situnamveke n’komwe pogwela m’coponyamoco. Koma Yesu wadziŵa ndalama zimene mzimayiyo waponyamo. Iye waponyamo tumakobili tuŵili tochedwa tumaleputa, tocepetsetsa pa ndalama zonse. Inde, tosakwana ngakhale kugula mpheta imodzi, imodzi mwa mbalame zocepa kwambili zimene zimagulitsidwa monga cakudya. Yesu wakondwela kwambili na mkazi wamasiye ameneyu. Conco aitana ophunzila ake na kuwaonetsa mkazi wamasiyeyu. Ndiyeno akuwauza kuti: “Mkazi wamasiye wosaukayu waponya zoculuka kuposa onse.” Kenako afotokoza kuti: “Cifukwa onsewo [maka-maka anthu olemela] aponya zimene atapa pa zoculuka zimene ali nazo, koma mayiyu, mu umphawi wake, waponya zonse zimene anali nazo, inde zonse zocilikizila moyo wake.” (Maliko 12:43, 44) Pamene mkazi wamasiye wokhulupilika ameneyu anapeleka ndalama yake yothela patsikulo, anaika moyo wake m’manja mwa Yehova kuti adzam’samalila.—Sal. 26:3. w21.04 6 ¶17-18
Cisanu, June 2
Taonani tsopano! Mwadzaza Yerusalemu yense ndi ciphunzitso canuci.—Mac. 5:28.
Yesu anakhalabe na maganizo oyenela pa utumiki wake wonse padziko lapansi. Ndipo amafuna kuti otsatila ake nawonso azikhala na maganizo oyenela pankhani ya ulaliki. (Yoh. 4:35, 36) Pamene Yesu anali na ophunzila ake, ophunzilawo anali kugwila nchito yolalikila mokangalika. (Luka 10:1, 5-11, 17) Koma pamene Yesu anamangidwa na kuphedwa, kwa kanthawi, cangu ca ophunzilawo panchito yolalikila cinacepa. (Yoh. 16:32) Ataukitsidwa, Yesu anawalimbikitsa kusumika maganizo awo pa ulaliki. Ndipo iye atabwelela kumwamba, ophunzilawo analalikila mwacangu cakuti adani awo anadandaula, monga mmene lemba la tsiku lalelo likuonetsela. Yesu anatsogolela panchito yolalikila imene Akhristu a m’nthawi ya atumwi anali kugwila. Ndipo Yehova anawadalitsa moti ciŵelengelo ca ophunzila cinawonjezeka. Mwacitsanzo, pa Pentekosite wa mu 33 C.E., anthu pafupi-fupi 3,000 anabatizidwa. (Mac. 2:41) Ndipo ciŵelengelo ca ophunzila cinapitiliza kukula modabwitsa. (Mac. 6:7) Yesu anali atakambilatu kuti nchito yolalikila idzacitika pamlingo waukulu m’masiku otsiliza.—Yoh. 14:12; Mac. 1:8. w21.05 14 ¶1-2