LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
Cilengezo
Taikaponso citundu cina: Togo Sign Language
  • Lelo

Sondo, May 24

Muvale umunthu watsopano.​—Aef. 4:24.

Mu Yesaya caputala 65, Yehova anafotokoza mmene zinthu zidzakhalile kwa anthu amene adzakhale m’paradaiso wauzimu. Mawuwo anakwanilitsidwa koyamba mu 537 B.C.E. Panthawiyo, Ayuda olapa anamasulidwa mu ukapolo ku Babulo, ndipo anabwelela ku dziko lawo. Yehova anadalitsa anthu ake, ndipo anawathandiza kukonza mzinda wowonongedwa wa Yerusalemu kuti ukhalenso wokongola. Anawathandizanso kubwezeletsa kacisi wake kuti akhalenso cimake ca kulambila koona. (Yes. 51:11; Zek. 8:3) Kukwanilitsidwa kwaciwili kwa ulosi wa Yesaya kunayamba mu 1919 C.E. pomwe alambili a Yehova amakono anamasulidwa ku ukapolo wa Babulo Wamkulu. Ndiyeno paradaiso wauzimu anayamba kukula kuzungulila dziko lonse lapansi. Alaliki a Ufumu okangalika anakhazikitsa mipingo ndipo anabala zipatso zauzimu. Amuna na akazi amene anali aciwawa komanso na makhalidwe aucinyama, anasintha n’kuvala “umunthu watsopano umene unalengedwa mogwilizana ndi cifunilo ca Mulungu.” w24.04 20-21 ¶3-4

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Mande, May 25

Aliyense ayenela kunyamula katundu wake.​—Agal. 6:5.

Ku maiko ena, makolo kapena acibale ena acikulile ni amene amasankhila munthu womanga naye banja. Koma kwina, acibale kapena mabwenzi amangokupezela munthu amene ungayambe naye cibwenzi. Iwo amalinganiza zakuti mukakumane kuti muone ngati ndinu oyenelelana. Mukapemphedwa kuti mupezele wina cibwenzi, kapena womanga naye banja, muziganizila zimene aliyense wa iwo akufuna. Mukapeza munthu amene muona kuti angakhale woyenelela, fufuzani zambili zokhudza umunthu wake na makhalidwe ake, koma maka-maka uzimu wake. Kukhala pa ubale wolimba na Yehova kumaposa ndalama, maphunzilo, ngakhale kuchuka. Komabe, kumbukilani kuti aŵiliwo ndiwo ayenela kupanga cisankho, kaya kukwatilana kapena ayi. w24.05 23 ¶11

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Ciwili, May 26

Mnzako weniweni amakusonyeza cikondi nthawi zonse.​—Miy. 17:17

Tingathandize amene ali pacibwenzi mwa zokamba zathu. Nthawi zina tingafunike kudziletsa kuti tisalankhule ciliconse. (Miy. 12:18) Mwacitsanzo, tingakhale ofunitsitsa kuuzako anzathu kuti uje na uje ali pacibwenzi, koma anthuwo angafune kukawauza okha za nkhaniyo. Sitiyenela kuwanenela misece amene ali pacibwenzi kapena kuwaimba mlandu pa nkhani zaumwini. (Miy. 20:19; Aroma 14:10; 1 Ates. 4:11) Kuwonjezela apo, sitiyenela kukamba mawu kapena kuwafunsa mafunso oonetsa kuti tikufuna kuti anthuwo akaloŵe m’banja.Nanga bwanji ngati amene ali pacibwenzi asankha kucithetsa? Tiyenela kupewa kuloŵelela m’nkhani zawo kapena kuimba mlandu mmodzi wa iwo. (1 Pet. 4:15) Ngati anthu athetsa cibwenzi sindiye kuti alakwitsa. Nthawi zambili kucita izi kumaonetsa kuti cibwenzico cakwanilitsa colinga cake, comwe ni kuthandiza amene ali pacibwenziwo kupanga cisankho coyenela. Komabe, cibwenzi cikatha, kaŵili-kawili anthuwo amakhala opwetekedwa mtima. Conco, tiyenela kupeza njila zowathandizila. w24.05 31 ¶15-16

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani