Cinai, April 9
Analowelelapo kuti athandize anthu.—Yes. 53:12.
Yehova anapempha Abulahamu kuti apeleke mwana wake Isaki nsembe. Izi ziyenela kuti zinamuvutitsa maganizo kwambili Abulahamu. Ngakhale n’telo, iye anali wofunitsitsa kumvela Yehova. Pamene Abulahamu anatsala pang’ono kupha mwana wake, Mulungu anamuletsa. Komabe citsanzoci cimaphunzitsa anthu onse okhulupilika zimene Yehova anali kudzacita m’tsogolo. Iye anali kudzalolela kupeleka nsembe Mwana wake wokondeka. Yehova anali kudzacita zimenezi cifukwa amakonda kwambili anthu. (Gen. 22:1-18) Patapita zaka zambili, Yehova anapatsa Aisiraeli Cilamulo. Mu Cilamulo cimeneco, Yehova anawauza kuti azipeleka nsembe zanyama kuti macimo awo azikhululukidwa. (Lev. 4:27-29; 17:11) Nsembe zimenezi zinali kuimila makonzedwe a nsembe yaikulu imene Mulungu analinganiza, yomwe inali kudzapulumutsa anthu ku ucimo kothelatu. Mulungu anauzila aneneli kulemba za mbewu yolonjezedwa. Mbewu imeneyi ni Mwana wa Mulungu wapadela, ndipo anali kudzavutika komanso kuphedwa kuti apulumutse anthu, kuphatikizapo inu, ku ucimo na imfa!—Yes. 53:1-12. w24.08 4 ¶7-8
Cisanu, April 10
Ndimakonda kwambili cilamulo canu! Ndimaganizila mozama cilamuloco tsiku lonse.—Sal. 119:97.
Poŵelenga Baibo, muziona mmene mungagwilitsile nchito zimene mwaŵelenga. Pamene mukuŵelenga Mawu a Mulungu, muzidzifunsa kuti, ‘Ningaseŵenzetse bwanji zimene naŵelengazi pali pano kapena m’tsogolo?’ Tiyelekeze kuti mwaŵelenga 1 Atesalonika 5:17, 18. Mutaŵelenga mavesi aŵili amenewa, mungadzifunse ngati mumapemphela pafupi-pafupi, komanso ngati mumapeleka mapemphelo ocokela pansi pa mtima. Kuwonjezela apo, mungaganizile zinthu zimene mumayamikila. Mwina mungaganizile kuti muyamikile Yehova pa zinthu zitatu. Ngakhale mutacita zimenezi kwa mphindi zocepa, kudzakuthandizani kuti mukhale munthu womva Mawu a Mulungu na kuwacita. Ganizilani mmene mungapindulile mukamacita zimenezi tsiku lililonse pamene muŵelenga Baibo! Kucita izi kudzakuthandizani kuti muzicita zimene Mawu a Mulungu amanena. w24.09 4-5 ¶9-10
Ciwelu, April 11
Samalani kuti musataye zinthu zimene tinakuthandizani kuti muzipeze nʼcolinga coti mudzalandile madalitso onse amene Mulungu wakukonzelani.—2 Yoh. 8.
Yehova anatilenga m’njila yapadela. Ngakhale kuti timasangalala tikalandila mphatso, timakhala na cimwemwe coculuka tikamapatsa ena. Timakhala acimwemwe tikakwanitsa kuthandiza okhulupilila anzathu. Ndipo timakondwela akatiyamikila pa zimene tacitazo. Komabe, kaya atiyamikile kapena ayi, timakhalabe acimwemwe podziŵa kuti tacita cinthu coyenela. Musaiŵale kuti zilizonse zimene mungapatse ena, “Yehova akhoza kukupatsani zambili kuposa zimenezo.” (2 Mbiri 25:9) Anthufe sitingathe kupatsa ena zambili kuposa zimene Yehova amatipatsa. Ndipo kulibe zosangalatsa kuposa zimene Yehova amatibwezela tikacitila ena zabwino. Conco tiyeni tisaleke kutengela citsanzo ca Atate wathu wa kumwamba ca kuwolowa manja. w24.09 31 ¶20-21