Sondo, August 2
Khristu ndiye kutha kwa Cilamulo.—Aroma. 10:4.
Titengapo phunzilo lofunika kwambili pa zimene mtumwi Paulo analembela Aheberi. Ena a iwo analeka kukula mwauzimu ndipo anafika ngakhale ‘poyambanso kufuna mkaka osati cakudya [cauzimu] cotafuna.’ (Aheb. 5:12) Iwo analephela kutsatila mfundo za coonadi zimene zinali kuvumbulidwa mwapang’ono-pang’ono kupitila mumpingo. (Miy. 4:18) Mwacitsanzo, Akhristu ambili Aciyuda anali kulimbikitsabe ena kutsatila Cilamulo ca Mose ngakhale kuti panali patapita zaka 30 pamene Cilamuloco cinathetsedwa pa maziko a nsembe ya Khristu. (Tito 1:10) Aliyense amene anaŵelengapo kalata youzilidwa ya mtumwi Paulo yopita kwa Aheberi angatsimikize kuti buku limeneli lili na cakudya cauzimu cotafuna. Cakudyaco n’cimene Akhristuwo anali kufunikila kuti alimbikitse cikhulupililo cawo cakuti kalambilidwe ka Cikhristu ni kopambana kuposa ka m’Cilamulo. Cakudyaco cinawathandizanso kukhala olimba mtima kuti apitilize kulalikila.—Aheb. 10:19-23. w24.04 6 ¶15
Mande, August 3
Mulungu adzaukitsa olungama ndi osalungama omwe.—Mac. 24:15.
Kungoyambila pamene Adamu na Hava anagwilizana na Satana popandukila ulamulilo wa Yehova Mulungu, anthu mabiliyoni amwalila. Kodi n’ciyani cimene cidzacitika kwa anthu amenewa? Kagulu kocepa ka otsatila a Khristu okhulupilika okwanila 144,000 kadzaukitsidwila ku moyo wosafa kumwamba. (Chiv. 14:1) Ndipo anthu oculuka amene anali kukonda Yehova, adzaukitsidwa pamene Yehova “adzaukitsa olungama.” Ndipo iwo adzalandila moyo wosatha padziko lapansi akadzakhalabe okhulupilika mu ulamulilo wa Khristu wa Zaka 1,000 komanso pa mayeso othela. (Dan. 12:13; Ahe. 12:1) Ndipo mu ulamulilo wa Zaka Cikwi, “osalungama”, kuphatikizapo omwe sanatumikilepo Yehova, ngakhale “amene ankacita zoipa,” adzapatsidwa mwayi wosintha njila zawo na kukhala okhulupilika. (Yoh. 5:29; Luka 23:42, 43) Komabe, anthu ena anali oipa zedi. Anthu otelowo, Yehova anaweluzilatu kuti sadzaukitsidwa.—Luka 12:4, 5. w24.05 2 ¶3; 5 ¶15; 6 ¶17
Ciwili, August 4
Amandilemekeza ndi milomo yawo yokha, koma mitima yawo aiika kutali ndi ine.—Yes. 29:13.
Munthu amene afuna kuyanjidwa na Yehova ayenela “kulankhula zoona mumtima mwake.” (Sal. 15:2) Izi sizitanthauza kungopewa kunama. Yehova amafuna kuti tikhale oona mtima m’zokamba na zocita zathu zonse. (Aheb. 13:18) Kukhala woona mtima n’kofunika “cifukwa Yehova amanyansidwa ndi munthu waciphamaso. Koma anthu owongoka mtima amakhala nawo pa ubwenzi wolimba.”(Miy. 3:32) Anthu amene ‘amalankhula zoona mumtima mwawo’ sadzionetsa ngati omvela pamaso pa anthu, koma n’kumaphwanya malamulo a Mulungu akakhala kwaokha. Amapewa kucita zinthu mwacinyengo. Munthu wacinyengo angayambe kuona kuti ena mwa malamulo a Yehova ni osathandiza. (Yak. 1:5-8) Iye angamaphwanye malamulowo pa nkhani zimene aona kuti n’zazing’ono. Ndipo akaona kuti kucita zimenezi sikunamubweletsele vuto lililonse, angakhale na cizolowezi cophwanya malamulo a Mulungu. Zotsatila zake, Yehova sangalandile kulambila kwake. (Mlal. 8:11) Koma ife sitiyenela kukhala otelo, tifunika kukhala oona mtima m’zinthu zonse. w24.06 10 ¶7-8