Cinai, May 14
Adzaweluza anthu okhala padziko lapansi mwacilungamo ndipo adzaweluza mitundu ya anthu mokhulupilika.—Sal. 96:13.
Kodi Yehova adzalilemekeza motani dzina lake posacedwa? Adzatelo mwa ziweluzo zake. Posacedwa, adzawononga Babulo Wamkulu cifukwa wabweletsa citonzo pa dzina lake loyela. (Chiv. 17:5, 16; 19:1, 2) Ena amene adzaone kuwonongedwa kwa Babulo Wamkulu, angadzasankhe kugwilizana nafe pa kulambila koona. Pamapeto pake, Yehova adzawononga dongosolo lonse la Satanali pa Aramagedo, ndi kucotsa onse amene amamutsutsa ndi kunyoza dzina lake. Koma adzapulumutsa onse amene amamukonda ndi kumumvela, amenenso amanyadila kumupatsa ulemelelo. (Maliko 8:38; 2 Ates. 1:6-10) Pambuyo pa ciyeso comaliza cimene cidzabwela pambuyo pa zaka 1,000 za ulamulilo wa Khristu, Yehova adzakhala atayeletsa dzina lake kothelatu. (Chiv. 20:7-10) Panthawi imeneyo, “dziko lapansi lidzadzaza ndi anthu odziwa ulemelelo wa Yehova, ngati mmene madzi amadzazila nyanja.” (Hab. 2:14) Zidzakhala zokondweletsa zedi pa nthawiyo pamene munthu aliyense adzapatse Yehova ulemelelo woyenelela dzina lake! w25.01 7 ¶15-16
Cisanu, May 15
Muyenela kupilila kuti muphunzitsidwe.—Aheb. 12:7.
N’ciyani cinali kudzathandiza Akhristu a Ciheberiwo kupilila pamene anali kuzunzidwa? Mtumwi Paulo anafuna kuthandiza Akhristuwo kuganizila mapindu amene akanapeza akapilila cizunzo. Conco, anawafotokozela kuti Akhristu akakumana na zinthu zoyesa cikhulupililo cawo, Mulungu angaseŵenzetse nthawi ya mayeselowo kuwaphunzitsa zinazake. Pa nthawiyo, iye angawathandize kukulitsa makhalidwe abwino a Cikhristu. Kuganizila mapindu amene akanapeza akapilila cizunzo, kukanathandiza Akhristuwo kupilila mosavuta. (Aheb. 12:11) Paulo analimbikitsa Akhristu a Ciheberi kukhala olimba mtima komanso kuti asalefuke pokumana na zinthu zoyesa cikhulupililo cawo. Iye anali pamalo abwino owalimbikitsa pa nkhani yopilila. Zinali conco cifukwa asanakhale Mkhristu, iye anali kuzunza Akhristu. Conco anali kumvetsa cizunzo cimene iwo anali kukumana naco. Anali kudziŵanso zimene munthu angacite kuti apilile cizunzo. Anali kudziŵa zimenezi cifukwa anakumana na mazunzo osiyana-siyana atakhala Mkhristu. 2 Akor. 11:23-25. w24.09 12-13 ¶16-17
Ciwelu, May 16
Pitilizani kukhala maso.—Mat. 25:13.
Tsiku lililonse likadutsa, tifunika kuwonjezela cangu cathu pa nchito yolalikila. Cifukwa ciyani? Cifukwa nthawi ikutha. Ganizilani zimene Yesu ananenelatu zokhudza nchito yolalikila m’masiku otsiliza, monga mmene lemba la Maliko 13:10 imakambila. Malinga na uthenga wa Mateyu pa nkhani imeneyi, Yesu anakamba kuti uthenga wabwino udzalalikidwa pa dziko lonse kumene kuli anthu “mapeto” asanafike. (Mat. 24:14) Mawu akuti mapeto amatanthauza kuthelatu kwa dongosolo loipali la Satana. Yehova anaikilatu “tsiku . . . ndi ola” limene zinthu zimenezi zidzacitika. (Mat. 24:36; Mac. 1:7) Tsiku lililonse limene ladutsa limatiyandikizitsa ku tsiku limenelo. (Aroma 13:11) Koma pakali pano tiyenela kupitiliza kulalikila mpaka mapeto adzafike. Pamene tikuganizila ulaliki wathu, tingacite bwino kudzisanthula na funso ili: N’cifukwa ciyani timalalikila uthenga wabwino? Kuyankha mwacidule, cikondi n’cimene cimatilimbikitsa. Zimene timacita pa nchito yolalikila zimaonetsa cikondi cathu pa uthenga wabwino, pa anthu, koma maka-maka pa Yehova na dzina lake. w24.05 14-15 ¶2-3