Citatu, April 29
Kuganiza bwino kudzakuyangʼanila, ndipo kuzindikila kudzakuteteza.—Miy. 2:11.
Tsiku lililonse timafunikila kupanga zisankho. Zisankho zina monga kusankha cakudya cam’mawa kapena nthawi yopita kukagona ndi zosavuta kupanga. Koma zina zimakhala zovuta. Zisankhozo zingakhudze thanzi lathu, cimwemwe cathu, okondedwa athu kapena ubwenzi wathu ndi Yehova. Timafuna kuti zisankho zimene tapanga zitipindulile ife eni komanso a m’banja mwathu. Koma koposa zonse, timafuna kuti zisankho zathu zizikondweletsa Yehova. (Aroma 12:1, 2) Sitepe imene munthu ayenela kutsatila kuti apange cisankho canzelu ndi kudziwa zoona zake zokhudza nkhaniyo. Zimenezi n’zofunika cifukwa ciyani? Tiyelekeze kuti munthu wapita kwa dokotala kukafunsa za matenda aakulu amene ali nawo. Kodi dokotala angapeleke mankhwala kwa munthuyo asanamupime kapena kumufunsako mafunso? Kutalitali! Mofanana ndi dokotala wabwino, inunso mungapange zisankho zanzelu ngati coyamba mumaganizila mfundo zonse zimene mwapeza zokhudzana ndi cisankho cimene mufuna kupanga. w25.01 14 ¶1-3
Cinai, April 30
Yehova wakukhululukila chimo lako ndipo suufa.—2 Sam. 12:13.
Tidziŵa ciyani ponena za cifundo ca Yehova? Kodi iye waonetsa bwanji kuti “sakufuna kuti munthu aliyense adzawonongedwe”? (2 Pet. 3:9) Ganizilani mmene anaonetsela cifundo cake kwa anthu amene anacitapo macimo akulu-akulu. Mfumu Davide anacitapo macimo akulu-akulu, kuphatikizapo cigololo komanso kupha munthu. Komabe Davide analapa, ndipo Yehova anam’khululukila. (2 Sam. 12:1-12) Mfumu Manase nayenso anacita zinthu zoipa kwambili kwa nthawi yaikulu ya moyo wake. Ngakhale kuti Manase anacita zoipa zambili, iye analapa ndipo Yehova anamucitila cifundo na kum’khululukila. (2 Mbiri 33:9-16) Zitsanzo zimenezi zitikumbutsa kuti Yehova amacita cifundo pakakhala cifukwa cocitila zimenezi. Iye adzaukitsa anthu ngati amenewa cifukwa iwo anazindikila kuti anacita macimo aakulu ndipo analapa. w24.05 4 ¶12
Cisanu, May 1
Mulungu alibe tsankho.—Aroma 2:11.
Yehova atapulumutsa anthu ake mu ukapolo ku Iguputo, anasankha ansembe kuti azitumikila pa cihema. Anasankhanso Alevi kuti azigwila nchito zina zopatulika za pa cihema. Koma kodi amene anali kutumikila pa cihema, kapena amene anali kukhala pafupi naco, anali kusamalidwa mwapadela? Ayi! Yehova alibe tsankho. Mwisiraeli aliyense anali na mwayi wokhala pa ubwenzi wabwino na Yehova. Mwacitsanzo, Yehova anaonetsetsa kuti mtundu wonse wa Isiraeli unali kutha kuona cipilala ca mtambo, komanso cipilala ca moto zomwe zinali kukhala pamwamba pa cihema. (Eks. 40:38) Mtambo ukayamba kuyenda, ngakhale amene anali kukhala kutali na cihema anali kutha kuuona, ndipo anali kusonkhanitsa katundu wawo, kupasula matenti awo, na kuyendela pamodzi na mtundu wonse wa Isiraeli. (Num. 9:15-23) N’cimodzi-modzinso masiku ano, mosasamala kanthu za kumene timakhala, Yehova akhoza kutisamalila na kutiteteza. w24.06 4 ¶10-12