Citatu, September 2
Yehova ali nafe. Musawaope.—Num. 14:9.
Tikakulitsa mantha oyenelela pa Yehova, timamukonda ngako, ndipo timapewa kucita ciliconse com’khumudwitsa. Ndife ofunitsitsa kudziŵa kusiyana pakati pa cabwino na coipa, komanso pakati pa coonadi na mabodza. Timafuna kucita izi kuti tikhale ovomelezeka kwa Yehova. (Miy. 2:3-6; Aheb. 5:14) Tikamaopa kwambili anthu kuposa mmene timaopela Mulungu, tingapatuke pa njila ya coonadi. Ganizilani citsanzo ca azondi 12 amene anapita kukazonda dziko limene Yehova analonjeza kupatsa Aisiraeli. Azondi 10 aja, mantha awo pa Akanani anali aakulu kuposa cikondi cawo pa Yehova. Iwo anauza Aisiraeli anzawo kuti: “Sitingathe kukalimbana nawo anthuwo, cifukwa ndi amphamvu kuposa ifeyo.” (Num. 13:27-31) M’kapenyedwe kaumunthu, Akanani anaonekadi amphamvu. Koma aliyense amene anakamba kuti Aisiraeli sakanatha kugonjetsa adani awo anali atamuiŵala Yehova. w24.07 9 ¶5-6
Cinai, September 3
Ndinu Woweluza wa dziko lonse lapansi. Ndiye kodi simuchita chilungamo?—Gen. 18:25.
Kodi ndife otsimikiza kuti Yehova nthawi zonse amaweluza anthu mwacilungamo? Inde! Abulahamu anamvetsa bwino kuti Yehova ni “Woweluza wa dziko lonse lapansi,” amene ni wangwilo, wanzelu zakuya, komanso wacifundo. Mulungu anaphunzitsa Mwana wake kuweluza, ndipo anam’patsa mphamvu zoweluza munthu aliyense. (Yoh. 5:22) Onse aŵili, Atate na Mwana, amatha kudziŵa za mumtima wa munthu aliyense. (Mat. 9:4) Conco, poweluza munthu aliyense, iwo ‘adzacita colungama’! Tiyeni tonse tikhulupilile na mtima wonse kuti kaweluzidwe ka Yehova n’kolungama. Tikuvomeleza kuti kuweluza si kwathu, koma n’kwa Yehova! (Yes. 55:8, 9) Conco na cidalilo conse, timasiya kuweluza konse m’manja mwake na Mwana wake, amene ni Mfumu yotengela cilungamo na cifundo ca Atate wake.—Yes. 11:3, 4. w24.05 7 ¶18-19
Cisanu, September 4
Yehova amanyansidwa ndi munthu waciphamaso, koma anthu owongoka mtima amakhala nawo paubwenzi wolimba.—Miy. 3:32.
Tingaphunzile zambili za kufunika kokhala oona mtima tikaganizila zimene zinacitika Yesu atakumana koyamba na Natanayeli. Pomwe Filipo anatenga mnzake Natanayeli kuti akaone Yesu, panacitika cinacake cocititsa cidwi. Yesu anali asanakumanepo na Natanayeli. Koma atamuona, ananena kuti: “Onani Mwisiraeli ndithu, amene mwa iye mulibe cinyengo.” (Yoh. 1:47) Yesu anaona kuti Natanayeli anali woona mtima mwapadela. Nayenso Natanayeli anali wopanda ungwilo ngati ife, Koma sanali kucita zacinyengo mwa njila ina iliyonse. Yesu anamunyadila Natanayeli na kumuyamikila cifukwa ca zimenezi. Zambili mwa zinthu zofunikila kuti tikondweletse Yehova zochulidwa mu Salimo 15, zikhudza mmene timacitila zinthu na ena. Pa Salimo 15:3 pamati mlendo m’tenti ya Yehova “sanena misece ndi lilime lake, sacitila mnzake coipa ciliconse, ndipo sanyoza anzake.” Kuseŵenzetsa molakwika mphatso ya kulankhula mwa njila imeneyi kungakhumudwitse ena.—Yak. 1:26. w24.06 10 ¶7, 9; 11 ¶10