LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Cisanu, September 4

Yehova amanyansidwa ndi munthu waciphamaso, koma anthu owongoka mtima amakhala nawo paubwenzi wolimba.​—Miy. 3:32.

Tingaphunzile zambili za kufunika kokhala oona mtima tikaganizila zimene zinacitika Yesu atakumana koyamba na Natanayeli. Pomwe Filipo anatenga mnzake Natanayeli kuti akaone Yesu, panacitika cinacake cocititsa cidwi. Yesu anali asanakumanepo na Natanayeli. Koma atamuona, ananena kuti: “Onani Mwisiraeli ndithu, amene mwa iye mulibe cinyengo.” (Yoh. 1:47) Yesu anaona kuti Natanayeli anali woona mtima mwapadela. Nayenso Natanayeli anali wopanda ungwilo ngati ife, Koma sanali kucita zacinyengo mwa njila ina iliyonse. Yesu anamunyadila Natanayeli na kumuyamikila cifukwa ca zimenezi. Zambili mwa zinthu zofunikila kuti tikondweletse Yehova zochulidwa mu Salimo 15, zikhudza mmene timacitila zinthu na ena. Pa Salimo 15:3 pamati mlendo m’tenti ya Yehova “sanena misece ndi lilime lake, sacitila mnzake coipa ciliconse, ndipo sanyoza anzake.” Kuseŵenzetsa molakwika mphatso ya kulankhula mwa njila imeneyi kungakhumudwitse ena.​—Yak. 1:26. w24.06 10 ¶7, 9; 11 ¶10

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Ciwelu, September 5

Ambuye, ngakhale ziwanda zimatigonjela tikagwilitsa nchito dzina lanu.​—Luka 10:17.

Mukaukonzekela mokwanila ulaliki wanu, simudzakhala ndi mantha kwambili pokamba ndi anthu. Yesu anakonzekeletsa ophunzila ake asanawatumize mu ulaliki. (Luka 10:​1-11) Cifukwa cosewenzetsa zimene Yesu anawaphunzitsa, ophunzilawo anapeza cimwemwe pa zimene anakwanitsa kucita. Kodi tingaukonzekele motani ulaliki? Tiyenela kuganizila mmene tingafotokozele coonadi mogwila mtima kwa ena m’mau athu-athu. Zimakhalanso bwino kuganizila njila ziwili kapena zitatu za mmene anthu angalandilile uthenga wathu. Kenaka tiziona mmene tingayankhile. Ndipo tikafikila munthu tizikhala odekha, tizimwetulila ndi kukhala waubwenzi. w24.04 16 ¶6-7

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Sondo, September 6

Ndinu woyenela, inu Yehova Mulungu wathu kulandila ulemelelo, ulemu ndi mphamvu cifukwa munalenga zinthu zonse.​—Chiv. 4:11.

Cifukwa copambana cimene timalalikila uthenga wabwino n’cakuti timamukonda Yehova Mulungu na dzina lake loyela. Timaona ulaliki wathu monga njila imene timatamandila Mulungu amene timam’konda. Timavomeleza na mtima kuti Yehova Mulungu ni woyenela kulandila ulemelelo, ulemu, na mphamvu kwa alambili ake okhulupilika. Timam’patsa ulemelelo na ulemu tikamauzako ena umboni wosatsutsika wakuti ‘analenga zinthu zonse’ komanso kuti tilipo cifukwa ca iye. Timam’patsa mphamvu, inde mphamvu zathu, tikamaseŵenzetsa nthawi yathu, mphamvu zathu, komanso zinthu zathu potengako mbali mokwanila m’nchito yolalikila malinga na mmene zinthu zilili kwa ife. (Mat. 6:33; Luka 13:24; Akol. 3:23) Mwacidule, tinganene kuti timakonda kukamba za Mulungu amene timakonda. Timalimbikitsidwanso kuuzako ena za dzina lake komanso zimene limatanthauza. w24.05 17 ¶11

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani