LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
Cilengezo
Taikaponso citundu cina: Sakalava
  • Lelo

Mande, August 31

Sungani misozi yanga mʼthumba lanu lacikopa.​—Sal. 56:8.

Paumoyo wake, Davide anafunika kupilila mavuto osiyanasiyana amene anamucititsa kuti agwetse misozi. Anacitilidwapo nkhanza na anthu ena komanso kugwilitsidwapo mwala na anthu amene anali kuwadalila. (1 Sam. 19:​10, 11; 2 Sam. 15:​10-14, 30) Panthawi ina, iye analemba kuti: “Ndafooka cifukwa ca kuusa moyo kwanga. Usiku wonse ndimanyowetsa bedi langa ndi misozi, ndimalila ndipo misozi imadzadza pabedi panga.” (Sal. 6:6) Ngakhale kuti Davide anakumana na mavuto onsewa, iye anali wotsimikiza kuti Yehova amamukonda. Analemba kuti: “Yehova adzamva mawu a kulila kwanga.” (Sal. 6:8) Mawu a mlemba lalelo amenewa, amationetsa kuti Yehova atikonda kwambili komanso kuti amasamala za ife. Davide anakamba kuti zinali monga Yehova akusunga misozi yake m’thumba kapena kuyalemba m’buku. Davide anali wotsimikiza kuti Yehova anali kuona mavuto amene anali kukumana nawo, komanso kuti anali kukumbukila ululu umene anali kumvela. Iye sanali kukaikila kuti Atate wake wacikondi wa kumwamba anali kudziŵa mavuto amene anali kukumana nawo komanso mmene anali kumukhudzila. w24.12 22 ¶11-12

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Ciwili, September 1

Pitilizani kudziyesa kuti muone ngati mukadali ndi cikhulupililo.​—2 Akor. 13:5.

Tonsefe tiyenela kuyesetsa kufika pa ucikulile wauzimu, komanso kucita zonse zotheka kuti tipitilize kukhala wacikulile mwauzimu. Izi zingatheke ngati tipewa kudzidalila. (1 Akor. 10:12) Tiyenela ‘kupitiliza kudziyesa’ kuti tione ngati tikupita patsogolo mwauzimu. M’kalata imene mtumwi Paulo analembela Akolose, anagogomeza kufunika kokhalabe wokhwima mwauzimu. Ngakhale kuti Akolose anali atakhala Akhristu okhwima, Paulo anawacenjeza kuti asagwele mu msampha wa kaganizidwe ka dziko. (Akol. 2:​6-10) Komanso Epafura, amene ayenela kuti anali kuwadziŵa bwino abale a mu mpingowo, anawapemphelela mosalekeza kuti ‘apitilize kukhala olimba mwauzimu’ kapena kuti okhwima. (Akol. 4:12) Mfundo yake ni yakuti onse aŵili, Paulo na Epafura, anadziŵa kuti kukhalabe wokhwima kumafuna kulimbikila, komanso thandizo la Mulungu. Iwo anali kufuna kuti Akolose akhalebe okhwima, kapena kuti afike pa ucikulile wauzimu mosasamala kanthu za mavuto amene anali kukumana nawo. w24.04 6-7 ¶16-17

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Citatu, September 2

Yehova ali nafe. Musawaope.​—Num. 14:9.

Tikakulitsa mantha oyenelela pa Yehova, timamukonda ngako, ndipo timapewa kucita ciliconse com’khumudwitsa. Ndife ofunitsitsa kudziŵa kusiyana pakati pa cabwino na coipa, komanso pakati pa coonadi na mabodza. Timafuna kucita izi kuti tikhale ovomelezeka kwa Yehova. (Miy. 2:​3-6; Aheb. 5:14) Tikamaopa kwambili anthu kuposa mmene timaopela Mulungu, tingapatuke pa njila ya coonadi. Ganizilani citsanzo ca azondi 12 amene anapita kukazonda dziko limene Yehova analonjeza kupatsa Aisiraeli. Azondi 10 aja, mantha awo pa Akanani anali aakulu kuposa cikondi cawo pa Yehova. Iwo anauza Aisiraeli anzawo kuti: “Sitingathe kukalimbana nawo anthuwo, cifukwa ndi amphamvu kuposa ifeyo.” (Num. 13:​27-31) M’kapenyedwe kaumunthu, Akanani anaonekadi amphamvu. Koma aliyense amene anakamba kuti Aisiraeli sakanatha kugonjetsa adani awo anali atamuiŵala Yehova. w24.07 9 ¶5-6

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani