LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Cinai, September 3

Ndinu Woweluza wa dziko lonse lapansi. Ndiye kodi simuchita chilungamo?​—Gen. 18:25.

Kodi ndife otsimikiza kuti Yehova nthawi zonse amaweluza anthu mwacilungamo? Inde! Abulahamu anamvetsa bwino kuti Yehova ni “Woweluza wa dziko lonse lapansi,” amene ni wangwilo, wanzelu zakuya, komanso wacifundo. Mulungu anaphunzitsa Mwana wake kuweluza, ndipo anam’patsa mphamvu zoweluza munthu aliyense. (Yoh. 5:22) Onse aŵili, Atate na Mwana, amatha kudziŵa za mumtima wa munthu aliyense. (Mat. 9:4) Conco, poweluza munthu aliyense, iwo ‘adzacita colungama’! Tiyeni tonse tikhulupilile na mtima wonse kuti kaweluzidwe ka Yehova n’kolungama. Tikuvomeleza kuti kuweluza si kwathu, koma n’kwa Yehova! (Yes. 55:​8, 9) Conco na cidalilo conse, timasiya kuweluza konse m’manja mwake na Mwana wake, amene ni Mfumu yotengela cilungamo na cifundo ca Atate wake.​—Yes. 11:​3, 4. w24.05 7 ¶18-19

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Cisanu, September 4

Yehova amanyansidwa ndi munthu waciphamaso, koma anthu owongoka mtima amakhala nawo paubwenzi wolimba.​—Miy. 3:32.

Tingaphunzile zambili za kufunika kokhala oona mtima tikaganizila zimene zinacitika Yesu atakumana koyamba na Natanayeli. Pomwe Filipo anatenga mnzake Natanayeli kuti akaone Yesu, panacitika cinacake cocititsa cidwi. Yesu anali asanakumanepo na Natanayeli. Koma atamuona, ananena kuti: “Onani Mwisiraeli ndithu, amene mwa iye mulibe cinyengo.” (Yoh. 1:47) Yesu anaona kuti Natanayeli anali woona mtima mwapadela. Nayenso Natanayeli anali wopanda ungwilo ngati ife, Koma sanali kucita zacinyengo mwa njila ina iliyonse. Yesu anamunyadila Natanayeli na kumuyamikila cifukwa ca zimenezi. Zambili mwa zinthu zofunikila kuti tikondweletse Yehova zochulidwa mu Salimo 15, zikhudza mmene timacitila zinthu na ena. Pa Salimo 15:3 pamati mlendo m’tenti ya Yehova “sanena misece ndi lilime lake, sacitila mnzake coipa ciliconse, ndipo sanyoza anzake.” Kuseŵenzetsa molakwika mphatso ya kulankhula mwa njila imeneyi kungakhumudwitse ena.​—Yak. 1:26. w24.06 10 ¶7, 9; 11 ¶10

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Ciwelu, September 5

Ambuye, ngakhale ziwanda zimatigonjela tikagwilitsa nchito dzina lanu.​—Luka 10:17.

Mukaukonzekela mokwanila ulaliki wanu, simudzakhala ndi mantha kwambili pokamba ndi anthu. Yesu anakonzekeletsa ophunzila ake asanawatumize mu ulaliki. (Luka 10:​1-11) Cifukwa cosewenzetsa zimene Yesu anawaphunzitsa, ophunzilawo anapeza cimwemwe pa zimene anakwanitsa kucita. Kodi tingaukonzekele motani ulaliki? Tiyenela kuganizila mmene tingafotokozele coonadi mogwila mtima kwa ena m’mau athu-athu. Zimakhalanso bwino kuganizila njila ziwili kapena zitatu za mmene anthu angalandilile uthenga wathu. Kenaka tiziona mmene tingayankhile. Ndipo tikafikila munthu tizikhala odekha, tizimwetulila ndi kukhala waubwenzi. w24.04 16 ¶6-7

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani