Sondo, August 30
Yehova ali pafupi ndi anthu a mtima wosweka.—Sal. 34:18.
Ngakhale kuti anthu ena anakucitilam’poni zinthu mwankhanza, dziŵani kuti Yehova amakukondani ndipo amakuonani kukhala wofunika. Conco, ngati mumadziona kukhala wosafunika, muzikumbukila kuti Yehova anaona zabwino mwa inu, ndipo anakukokelani kwa iye. (Yoh. 6:44) Ni wokonzeka kukuthandizani nthawi zonse cifukwa ndinu wofunika kwa iye. Kukambilana citsanzo ca Yesu kungatithandize kudziŵa mmene Yehova amawaonela anthu osweka mtima. Pamene anali kucita utumiki wake wa padziko lapansi, anaona mmene ena anali kucitila zinthu na anthu amene anali kuoneka onyozeka. Koma iye anacita nawo mokoma mtima anthu onyozekawo. (Mat. 9:9-12) Pamene mayi wodwala matenda oopsa kwambili anagwila covala ca Yesu, ali na cidalilo cakuti adzacila, Yesu anamutonthoza na kumuyamikila kaamba ka cikhulupililo cake. (Maliko 5:25-34) Yesu amaonetsa bwino makhalidwe a Atate wake. (Yoh. 14:9) Conco, musakaikile zakuti Yehova amakuonani kukhala wofunika, komanso kuti amaona makhalidwe anu abwino, kuphatikizapo cikhulupililo canu, na cikondi canu pa iye. w24.10 7 ¶4-5
Mande, August 31
Sungani misozi yanga mʼthumba lanu lacikopa.—Sal. 56:8.
Paumoyo wake, Davide anafunika kupilila mavuto osiyanasiyana amene anamucititsa kuti agwetse misozi. Anacitilidwapo nkhanza na anthu ena komanso kugwilitsidwapo mwala na anthu amene anali kuwadalila. (1 Sam. 19:10, 11; 2 Sam. 15:10-14, 30) Panthawi ina, iye analemba kuti: “Ndafooka cifukwa ca kuusa moyo kwanga. Usiku wonse ndimanyowetsa bedi langa ndi misozi, ndimalila ndipo misozi imadzadza pabedi panga.” (Sal. 6:6) Ngakhale kuti Davide anakumana na mavuto onsewa, iye anali wotsimikiza kuti Yehova amamukonda. Analemba kuti: “Yehova adzamva mawu a kulila kwanga.” (Sal. 6:8) Mawu a mlemba lalelo amenewa, amationetsa kuti Yehova atikonda kwambili komanso kuti amasamala za ife. Davide anakamba kuti zinali monga Yehova akusunga misozi yake m’thumba kapena kuyalemba m’buku. Davide anali wotsimikiza kuti Yehova anali kuona mavuto amene anali kukumana nawo, komanso kuti anali kukumbukila ululu umene anali kumvela. Iye sanali kukaikila kuti Atate wake wacikondi wa kumwamba anali kudziŵa mavuto amene anali kukumana nawo komanso mmene anali kumukhudzila. w24.12 22 ¶11-12
Ciwili, September 1
Pitilizani kudziyesa kuti muone ngati mukadali ndi cikhulupililo.—2 Akor. 13:5.
Tonsefe tiyenela kuyesetsa kufika pa ucikulile wauzimu, komanso kucita zonse zotheka kuti tipitilize kukhala wacikulile mwauzimu. Izi zingatheke ngati tipewa kudzidalila. (1 Akor. 10:12) Tiyenela ‘kupitiliza kudziyesa’ kuti tione ngati tikupita patsogolo mwauzimu. M’kalata imene mtumwi Paulo analembela Akolose, anagogomeza kufunika kokhalabe wokhwima mwauzimu. Ngakhale kuti Akolose anali atakhala Akhristu okhwima, Paulo anawacenjeza kuti asagwele mu msampha wa kaganizidwe ka dziko. (Akol. 2:6-10) Komanso Epafura, amene ayenela kuti anali kuwadziŵa bwino abale a mu mpingowo, anawapemphelela mosalekeza kuti ‘apitilize kukhala olimba mwauzimu’ kapena kuti okhwima. (Akol. 4:12) Mfundo yake ni yakuti onse aŵili, Paulo na Epafura, anadziŵa kuti kukhalabe wokhwima kumafuna kulimbikila, komanso thandizo la Mulungu. Iwo anali kufuna kuti Akolose akhalebe okhwima, kapena kuti afike pa ucikulile wauzimu mosasamala kanthu za mavuto amene anali kukumana nawo. w24.04 6-7 ¶16-17