LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
Cilengezo
Taikaponso citundu cina: Sakalava
  • Lelo

Ciwili, September 1

Pitilizani kudziyesa kuti muone ngati mukadali ndi cikhulupililo.​—2 Akor. 13:5.

Tonsefe tiyenela kuyesetsa kufika pa ucikulile wauzimu, komanso kucita zonse zotheka kuti tipitilize kukhala wacikulile mwauzimu. Izi zingatheke ngati tipewa kudzidalila. (1 Akor. 10:12) Tiyenela ‘kupitiliza kudziyesa’ kuti tione ngati tikupita patsogolo mwauzimu. M’kalata imene mtumwi Paulo analembela Akolose, anagogomeza kufunika kokhalabe wokhwima mwauzimu. Ngakhale kuti Akolose anali atakhala Akhristu okhwima, Paulo anawacenjeza kuti asagwele mu msampha wa kaganizidwe ka dziko. (Akol. 2:​6-10) Komanso Epafura, amene ayenela kuti anali kuwadziŵa bwino abale a mu mpingowo, anawapemphelela mosalekeza kuti ‘apitilize kukhala olimba mwauzimu’ kapena kuti okhwima. (Akol. 4:12) Mfundo yake ni yakuti onse aŵili, Paulo na Epafura, anadziŵa kuti kukhalabe wokhwima kumafuna kulimbikila, komanso thandizo la Mulungu. Iwo anali kufuna kuti Akolose akhalebe okhwima, kapena kuti afike pa ucikulile wauzimu mosasamala kanthu za mavuto amene anali kukumana nawo. w24.04 6-7 ¶16-17

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Citatu, September 2

Yehova ali nafe. Musawaope.​—Num. 14:9.

Tikakulitsa mantha oyenelela pa Yehova, timamukonda ngako, ndipo timapewa kucita ciliconse com’khumudwitsa. Ndife ofunitsitsa kudziŵa kusiyana pakati pa cabwino na coipa, komanso pakati pa coonadi na mabodza. Timafuna kucita izi kuti tikhale ovomelezeka kwa Yehova. (Miy. 2:​3-6; Aheb. 5:14) Tikamaopa kwambili anthu kuposa mmene timaopela Mulungu, tingapatuke pa njila ya coonadi. Ganizilani citsanzo ca azondi 12 amene anapita kukazonda dziko limene Yehova analonjeza kupatsa Aisiraeli. Azondi 10 aja, mantha awo pa Akanani anali aakulu kuposa cikondi cawo pa Yehova. Iwo anauza Aisiraeli anzawo kuti: “Sitingathe kukalimbana nawo anthuwo, cifukwa ndi amphamvu kuposa ifeyo.” (Num. 13:​27-31) M’kapenyedwe kaumunthu, Akanani anaonekadi amphamvu. Koma aliyense amene anakamba kuti Aisiraeli sakanatha kugonjetsa adani awo anali atamuiŵala Yehova. w24.07 9 ¶5-6

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Cinai, September 3

Ndinu Woweluza wa dziko lonse lapansi. Ndiye kodi simuchita chilungamo?​—Gen. 18:25.

Kodi ndife otsimikiza kuti Yehova nthawi zonse amaweluza anthu mwacilungamo? Inde! Abulahamu anamvetsa bwino kuti Yehova ni “Woweluza wa dziko lonse lapansi,” amene ni wangwilo, wanzelu zakuya, komanso wacifundo. Mulungu anaphunzitsa Mwana wake kuweluza, ndipo anam’patsa mphamvu zoweluza munthu aliyense. (Yoh. 5:22) Onse aŵili, Atate na Mwana, amatha kudziŵa za mumtima wa munthu aliyense. (Mat. 9:4) Conco, poweluza munthu aliyense, iwo ‘adzacita colungama’! Tiyeni tonse tikhulupilile na mtima wonse kuti kaweluzidwe ka Yehova n’kolungama. Tikuvomeleza kuti kuweluza si kwathu, koma n’kwa Yehova! (Yes. 55:​8, 9) Conco na cidalilo conse, timasiya kuweluza konse m’manja mwake na Mwana wake, amene ni Mfumu yotengela cilungamo na cifundo ca Atate wake.​—Yes. 11:​3, 4. w24.05 7 ¶18-19

Kusanthula Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani