Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2026)
Tulukani
Lowani
Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
Chilengezo
Chinenero chatsopano chomwe chilipo: Sakalava
  • Lero

Lachiwiri, September 1

Pitirizani kudziyesa kuti muone ngati mukadali ndi chikhulupiriro.—2 Akor. 13:5.

Sikuti tizingoyesetsa kuti tikule mwauzimu koma tiziyesetsanso kuti tikhalebe aakulu mwauzimu. Kuti zimenezi zitheke tiyenera kupewa kudzidalira. (1 Akor. 10:12) Tifunika “kupitiriza kudziyesa” kuti tione ngati tikupitabe patsogolo. M’kalata yake yopita kwa Akhristu a ku Kolose, mtumwi Paulo anatsindika kufunika kokhalabe olimba mwauzimu. Ngakhale kuti iwo anali aakulu kale mwauzimu, Paulo anawachenjeza kuti asapusitsidwe ndi nzeru za anthu. (Akol. 2:​6-10) Epafura, yemwe zikuoneka kuti ankawadziwa bwino anthu a mumpingomo, ankawapempherera nthawi zonse kuti “apitirize kukhala olimba mwauzimu.” (Akol. 4:12) Kodi tikuphunzirapo chiyani? Paulo ndi Epafura ankadziwa kuti pamafunika khama komanso kuthandizidwa ndi Mulungu kuti munthu akhalebe wolimba mwauzimu. Iwo ankafuna kuti Akhristu a ku Kolose akhalebe olimba mwauzimu ngakhale kuti ankakumana ndi mavuto. w24.04 14:16-17

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Lachitatu, September 2

Yehova ali nafe. Musawaope.—Num. 14:9.

Kuopa Yehova moyenera kumatithandiza kuti tizimukonda kwambiri moti sitingachite chilichonse chimene chingamukhumudwitse. Timafunitsitsa kuphunzira kuti tizitha kusiyanitsa pakati pa zoyenera ndi zosayenera ndiponso pakati pa choonadi ndi mfundo zabodza n’cholinga choti tizisangalatsa Yehova. (Miy. 2:​3-6; Aheb. 5:14) Tikamaopa kwambiri anthu kuposa Mulungu tikhoza kupatutsidwa pa choonadi. Chitsanzo pa nkhaniyi ndi atsogoleri amafuko 12 amene anapita kukaona dziko limene Mulungu analonjeza kuti adzapereka kwa Aisiraeli. Atsogoleri 10 ankaopa kwambiri Akanani kuposa mmene ankakondera Yehova. Iwo anauza Aisiraeli anzawo kuti: “Sitingathe kukalimbana nawo anthuwo, chifukwa ndi amphamvu kuposa ifeyo.” (Num. 13:​27-31) N’zoona kuti malinga n’kuona kwa anthu, Akanani anali amphamvu kuposa Aisiraeli. Koma ponena kuti Aisiraeli sakanatha kugonjetsa adani awo ndiye kuti sankaganizira za Yehova. w24.07 28:5-6

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Lachinayi, September 3

Ndinu Woweruza wa dziko lonse lapansi. Ndiye kodi simuchita chilungamo?—Gen. 18:25.

Kodi tingakhale otsimikiza kuti nthawi zonse Yehova amaweruza anthu mwachilungamo? Inde. Abulahamu ankadziwa kuti Yehova ndi “Woweruza wa dziko lonse lapansi” yemwe ndi wangwiro, wanzeru komanso wachifundo. Iye waphunzitsa bwino Mwana wake ndipo wamupatsa udindo wonse woweruza. (Yoh. 5:22) Iye pamodzi ndi Mwana wakeyu amadziwa zimene zili mumtima mwa munthu. (Mat. 9:4) Choncho akamadzaweruza munthu aliyense adzachita zinthu ‘mwachilungamo.’ Tiyeni tisamakayikire ngakhale pang’ono kuti Yehova amadziwa zonse. Timadziwa kuti iye ndi woyenera kuweruza osati ifeyo. (Yes. 55:​8, 9) Choncho nkhani yonse yoweruzayi timaisiya m’manja mwa iyeyo ndi Mwana wake. Ndipo Mwana wakeyu ndi Mfumu imene imatsanzira Atate wake posonyeza chilungamo ndi chifundo.—Yes. 11:​3, 4. w24.05 18:18-19

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani