Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2026)
Tulukani
Lowani
Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Lero

Lachitatu, September 2

Yehova ali nafe. Musawaope.—Num. 14:9.

Kuopa Yehova moyenera kumatithandiza kuti tizimukonda kwambiri moti sitingachite chilichonse chimene chingamukhumudwitse. Timafunitsitsa kuphunzira kuti tizitha kusiyanitsa pakati pa zoyenera ndi zosayenera ndiponso pakati pa choonadi ndi mfundo zabodza n’cholinga choti tizisangalatsa Yehova. (Miy. 2:​3-6; Aheb. 5:14) Tikamaopa kwambiri anthu kuposa Mulungu tikhoza kupatutsidwa pa choonadi. Chitsanzo pa nkhaniyi ndi atsogoleri amafuko 12 amene anapita kukaona dziko limene Mulungu analonjeza kuti adzapereka kwa Aisiraeli. Atsogoleri 10 ankaopa kwambiri Akanani kuposa mmene ankakondera Yehova. Iwo anauza Aisiraeli anzawo kuti: “Sitingathe kukalimbana nawo anthuwo, chifukwa ndi amphamvu kuposa ifeyo.” (Num. 13:​27-31) N’zoona kuti malinga n’kuona kwa anthu, Akanani anali amphamvu kuposa Aisiraeli. Koma ponena kuti Aisiraeli sakanatha kugonjetsa adani awo ndiye kuti sankaganizira za Yehova. w24.07 28:5-6

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Lachinayi, September 3

Ndinu Woweruza wa dziko lonse lapansi. Ndiye kodi simuchita chilungamo?—Gen. 18:25.

Kodi tingakhale otsimikiza kuti nthawi zonse Yehova amaweruza anthu mwachilungamo? Inde. Abulahamu ankadziwa kuti Yehova ndi “Woweruza wa dziko lonse lapansi” yemwe ndi wangwiro, wanzeru komanso wachifundo. Iye waphunzitsa bwino Mwana wake ndipo wamupatsa udindo wonse woweruza. (Yoh. 5:22) Iye pamodzi ndi Mwana wakeyu amadziwa zimene zili mumtima mwa munthu. (Mat. 9:4) Choncho akamadzaweruza munthu aliyense adzachita zinthu ‘mwachilungamo.’ Tiyeni tisamakayikire ngakhale pang’ono kuti Yehova amadziwa zonse. Timadziwa kuti iye ndi woyenera kuweruza osati ifeyo. (Yes. 55:​8, 9) Choncho nkhani yonse yoweruzayi timaisiya m’manja mwa iyeyo ndi Mwana wake. Ndipo Mwana wakeyu ndi Mfumu imene imatsanzira Atate wake posonyeza chilungamo ndi chifundo.—Yes. 11:​3, 4. w24.05 18:18-19

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026

Lachisanu, September 4

Yehova amanyansidwa ndi munthu wachiphamaso, koma anthu owongoka mtima amakhala nawo pa ubwenzi wolimba.—Miy. 3:32.

Tingathe kuona ubwino wokhala oona mtima tikaganizira zimene zinachitika Yesu atakumana koyamba ndi Natanayeli. Filipo atamubweretsa Natanayeli kwa Yesu, panachitika chinthu china chochititsa chidwi. Ngakhale kuti Yesu anali asanakumanepo ndi Natanayeli, iye ananena kuti: “Onani Mwisiraeli ndithu, amene mwa iye mulibe chinyengo.” (Yoh. 1:47) Yesu anaona kuti Natanayeli anali woona mtima kwambiri. Mofanana ndi tonsefe, Natanayeli sanali wangwiro koma ankayesetsa kupewa chinyengo. Yesu anachita chidwi ndi zimenezi ndipo anayamikira Natanayeli. Mfundo zambiri za mu Salimo 15 zimakhudza mmene timachitira zinthu ndi anzathu. Salimo 15:3 limanena kuti mlendo mutenti ya Yehova “sanena miseche ndi lilime lake, sachitira mnzake choipa chilichonse, ndipo sanyoza anzake.” Kugwiritsa ntchito mawu athu molakwika kungavulaze ena.—Yak. 1:26. w24.06 24:7, 9-10

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2026
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2026 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani