36 “Bezaleli komanso Oholiabu+ ndi mwamuna aliyense wa mtima wanzeru amene Yehova wam’patsa nzeru+ ndi kuzindikira+ pa zinthu zimenezi, ayenera kugwira ntchitoyi. Iwowa apatsidwa nzeru ndi kuzindikira kuti adziwe kuchita ntchito zonse zopatulika motsatira zonse zimene Yehova walamula.”+