Lachinayi, December 25
Valani chikondi, chifukwa chimagwirizanitsa anthu mwamphamvu kwambiri kuposa chinthu china chilichonse.—Akol. 3:14.
Kodi tingasonyeze bwanji kuti timakonda abale ndi alongo athu? Njira imodzi ndi kuwalimbikitsa kapena kuwatonthoza. Chifundo ndi chimene chingatichititse kuti ‘tipitirize kulimbikitsana.’ (1 Ates. 4:18) Kodi tingatani kuti tizikonda kwambiri abale athu? Tingatero poyesetsa kuti tiziwakhululukira zimene amalakwitsa. N’chifukwa chiyani n’zofunika kuti tizikondana kwambiri masiku ano? Petulo anapereka chifukwa chake pomwe ananena kuti: “Mapeto a zinthu zonse ayandikira. Choncho . . . muzikondana kwambiri.” (1 Pet. 4:7, 8) Kodi chichitike n’chiyani pamene mapeto akuyandikira kwambiri? Ponena za otsatira ake, Yesu ananena kuti: “Anthu a mitundu yonse adzadana nanu chifukwa cha dzina langa.” (Mat. 24:9) Kuti tithe kupirira tiyenera kumagwirizana kwambiri. Tikatero, Satana sadzatha kutigawanitsa chifukwa chakuti tili ndi chikondi chimene chimatigwirizanitsa pamodzi.—Afil. 2:1, 2. w23.11 13 ¶18-19
Lachisanu, December 26
Ndife antchito anzake a Mulungu.—1 Akor. 3:9.
Choonadi cha Mawu a Mulungu ndi champhamvu kwambiri. Tikamaphunzitsa anthu zoona zokhudza Yehova komanso mmene alili, pamachitika chinthu china chodabwitsa. Khungu limene Satana amachititsa m’maganizo mwa anthu limayamba kuchoka ndipo amayamba kuona makhalidwe abwino a Atate athu okondedwa, ngati mmene ifeyo timachitira. Iwo amagoma ndi mphamvu zake zopanda malire. (Yes. 40:26) Amayamba kumukhulupirira chifukwa amaona kuti ndi wachilungamo. (Deut. 32:4) Amaphunzira zambiri zokhudza nzeru zake zapamwamba. (Yes. 55:9; Aroma 11:33) Amalimbikitsidwanso kudziwa kuti iyeyo ndi chikondi. (1 Yoh. 4:8) Akayamba kukhala naye pa ubwenzi, chiyembekezo chawo chodzakhala ndi moyo mpaka kalekale monga ana ake, chimakhala chotsimikizika. Tilitu ndi mwayi waukulu kwambiri wothandiza anthu kuti akhale pa ubwenzi ndi Atate wawo. Tikamachita zimenezi, Yehova amationa kuti ndife “antchito anzake.”—1 Akor. 3:5. w24.02 12 ¶15
Loweruka, December 27
Ndi bwino kuti usalonjeze kusiyana ndi kulonjeza koma osakwaniritsa zimene walonjezazo.—Mlal. 5:5.
Ngati mukuphunzira Baibulo kapena makolo anu ndi a Mboni, n’kutheka kuti mukuganizira zobatizidwa. Chimenechitu ndi cholinga chabwino kwambiri. Komabe musanabatizidwe, muyenera kudzipereka kwa Yehova. Kodi munthu amadzipereka bwanji kwa Yehova? Amamulonjeza m’pemphero kuti azilambira iye yekha komanso kuti aziika zimene Yehovayo amafuna pamalo oyamba. Apa amakhala akulonjeza Yehova kuti adzapitiriza kumukonda ndi ‘mtima wake wonse, moyo wake wonse, maganizo ake onse ndi mphamvu zake zonse.’ (Maliko 12:30) Munthu amadzipereka ali kwayekha ndipo imakhala nkhani ya pakati pa iyeyo ndi Yehova. Koma kubatizidwa kumachitika pagulu ndipo kumatsimikizira ena kuti munthuyo anadzipereka. Kudzipereka ndi lonjezo lopatulika ndipo mumafunika kumalikwaniritsa. Nayenso Yehova amayembekezera kuti muzilikwaniritsa.—Mlal. 5:4. w24.03 2 ¶2; 3 ¶5