Lachinayi, March 23
Khalani mwamtendere ndi anthu onse.—Aroma 12:18.
Kodi tiyenera kuchita chiyani tikazindikira kuti takhumudwitsa Mkhristu mnzathu? Tiyenera kupemphera kwa Yehova mochokera pansi pamtima. Tingamupemphe kuti atithandize pamene tikuyesetsa kuti tikhalenso pamtendere ndi m’bale wathuyo. Tingachitenso bwino kudzifufuza. Tingadzifunse mafunso ngati awa: ‘Kodi ndimavomereza ndikalakwitsa zinthu, n’kupepesa modzichepetsa komanso kukhazikitsa mtendere? Kodi Yehova ndi Yesu amamva bwanji ndikamayesetsa kukhazikitsa mtendere ndi m’bale kapena mlongo?’ Mayankho athu pamafunso amenewa angatilimbikitse kumvera Yesu ndipo modzichepetsa tingapite kukakambirana ndi Mkhristu mnzathuyo kuti tikhale nayenso pamtendere. Tikapita kukakhazikitsa mtendere ndi m’bale wathu timafunika kukhala odzichepetsa. (Aef. 4:2, 3) Tiyenera kupita kwa munthu amene tamukhumudwitsayo n’cholinga choti tikhalenso naye pa ubwenzi wabwino. Kumbukirani kuti kukhazikitsa mtendere ndi m’bale wanuyo n’kofunika kwambiri kuposa kufufuza yemwe analakwa ndi yemwe sanalakwe.—1 Akor. 6:7. w21.12 26 ¶13-16
Lachisanu, March 24
Anaona mzindawo n’kuyamba kuulirira.—Luka 19:41.
Yesu anamva kupweteka mumtima chifukwa Ayuda ambiri anali atasonyeza kuti sankafuna kumvetsera uthenga wa Ufumu. Chifukwa cha zimenezi, mzinda wa Yerusalemu ukanawonongedwa ndipo Ayuda omwe akanapulumuka akanatengedwa kupita ku ukapolo. (Luka 21:20-24) N’zomvetsa chisoni kuti monga mmene iye ananenera, anthu ambiri anamukanadi. Kodi anthu ambiri kudera limene mumakhala amamvetsera uthenga wa Ufumu? Ngati ndi anthu ochepa amene amamvetsera mukamayesetsa kuwaphunzitsa choonadi, kodi mungaphunzire chiyani pa misozi ya Yesu? Yehova amadera nkhawa anthu. Misozi ya Yesu imatikumbutsa kuti Yehova amaganizira kwambiri anthu. “Safuna kuti wina aliyense adzawonongedwe, koma amafuna kuti anthu onse alape.” (2 Pet. 3:9) Masiku ano timasonyeza kuti timakonda anthu ena poyesetsa kuwathandiza kuti amve uthenga wabwino wa Ufumu.—Mat. 22:39. w22.01 16 ¶10-12
Loweruka, March 25
Ndakulondolani kulikonse, dzanja lanu lamanja landigwira mwamphamvu.—Sal. 63:8.
Chikhulupiriro chanu chingalimbe kwambiri mukamaganizira zimene Yehova wachitira anthu ake komanso zimene wakuchitirani inuyo panokha. Chofunika kwambiri ndi chakuti, mudzayamba kukonda kwambiri Yehova. Kuposa makhalidwe ena onse, chikondi chingakuthandizeni kuti muzimvera Yehova, kulolera kusiya zinthu zina kuti mumusangalatse komanso kupirira mayesero alionse. (Mat. 22:37-39; 1 Akor. 13:4, 7; 1 Yoh. 5:3) Palibe chinthu china chofunika kwambiri kuposa kukonda komanso kukhala pa ubwenzi ndi Yehova. (Sal. 63:1-7) Muzikumbukira kuti kupemphera, kuphunzira komanso kuganizira mozama zimene tikuphunzirazo ndi mbali ya kulambira kwathu. Mofanana ndi Yesu, muzipeza malo opanda phokoso kuti muchite zinthu ndi Yehova. Muzipewa zilizonse zimene zingakusokonezeni. Muzipempha Yehova kuti akuthandizeni kuika maganizo anu onse pa zinthu zokhudza kulambira zomwe mukuchita. Mukamagwiritsa ntchito bwino nthawi yanu panopa, Yehova adzakudalitsani ndipo mudzakhala ndi moyo m’dziko latsopano la Mulungu mpaka kalekale.—Maliko 4:24. w22.01 31 ¶18-20