Lachinayi, July 16
Tayeretsedwa . . . kudzera mʼthupi la Yesu Khristu limene analipereka nsembe kamodzi kokha.—Aheb. 10:10.
Mogwirizana ndi zimene Baibulo limanena, dipo ndi malipiro amene amaperekedwa pofuna kuphimba machimo komanso kugwirizanitsa anthu ndi Yehova. Yehova amaona kuti dipo ndi limene limathandiza kubwezeretsa zimene zinatayika. Kumbukirani kuti Adamu ndi Hava anataya moyo wangwiro komanso mwayi wokhala ndi moyo wosatha. Choncho dipo linayenera kukhala malipiro ofanana ndi zimene zinatayikazo. (1 Tim. 2:6) Linayenera kuperekedwa ndi munthu wamkulu yemwe (1) anali wangwiro, (2) anali ndi mwayi woti akanatha kukhala ndi moyo padziko lapansi mpaka kalekale komanso (3) anali wofunitsitsa kupereka moyo wake ngati nsembe. Taonani zifukwa zitatu zimene zikuchititsa Yesu kukhala woyenera kupereka dipoli. (1) Iye anali wangwiro ndipo “sanachite tchimo.” (1 Pet. 2:22) (2) Popeza anali wangwiro, akanatha kukhala ndi moyo mpaka kalekale padziko lapansi. (3) Iye analolera kufa n’kupereka moyo wake chifukwa cha ifeyo.—Aheb. 10:9. w25.02 4-5 ¶11-12
Lachisanu, July 17
Iye akafuna kupereka mzimu sapereka moumira.—Yoh. 3:34.
Yehova amakukondani ndipo amafuna kuti mukhale m’banja lake. Izitu zili choncho ngakhale kuti mukukumana ndi mavuto omwe angakulepheretseni kubatizidwa. Pa nthawi ina Yesu anauza kagulu ka ophunzira ake kuti: “Ngati mutakhala ndi chikhulupiriro chofanana ndi kanjere ka mpiru kuchepa kwake, mudzatha kuuza phiri ili kuti, ‘Choka pano upite apo,’ ndipo lidzachokadi. Palibe chimene chidzakhale chosatheka kwa inu.” (Mat. 17:20) Anthu amene anamva zimenezi anali atakhala ndi Yesu kwa zaka zochepa chabe, choncho chikhulupiriro chawo chinali chikukulabe. Koma Yesu anawatsimikizira kuti ngati atakhala ndi chikhulupiriro chokwanira, Yehova adzawathandiza kulimbana ndi mavuto okhala ngati mapiri. Ndipotu Yehova angakuthandizeni inunso kuchita zimenezi. Ngati mwazindikira kuti pali mavuto ena omwe akukulepheretsani kubatizidwa, yesetsani kuti muwathetse mofulumira. Dziperekeni kwa Yehova ndi kubatizidwa. Mukachita zimenezi mudzakhala kuti mwasankha bwino kwambiri. w25.03 7 ¶18-20
Loweruka, July 18
Yehova ali kumbali yanga, sindidzaopa.—Sal. 118:6.
Tingathe kupirira mayesero ngati timakumbukira kuti Mulungu wamoyo ndi wokonzeka kutithandiza. Tingamakhulupirire kwambiri zimenezi tikaganizira zimene anachitapo kale. (Yes. 37:17, 33-37) Komanso muziwerenga ndi kuonera malipoti a pa jw.org osonyeza mmene Yehova akuthandizira abale ndi alongo athu masiku ano. Kuwonjezera pamenepo, muziganiziranso mmene anakuthandizirani inuyo. Zilibe kanthu kuti simungatchule mavuto akuluakulu. Tikutero chifukwa Yehova wakhala akukuchitirani zambiri pa moyo wanu. Anakukokani kuti mukhale naye pa ubwenzi. (Yoh. 6:44) Choncho mungachite bwino kumupempha kuti akukumbutseni nthawi imene anayankha mapemphero anu, kukuthandizani pa nthawi yoyenera komanso kukusamalirani pa nthawi yovuta. Kuganizira zimenezi kungakuthandizeni kuti muzikhulupirira kwambiri kuti Yehova adzapitiriza kukuthandizani. w24.06 21 ¶8