Lachinayi, June 4
Anthu a ku Nineve adzauka pa Tsiku la Chiweruzo.—Mat. 12:41.
Mulungu anakumbutsa Yona kuti anthu a ku Nineve ‘sankadziwa kusiyanitsa zoyenera ndi zolakwika.’ (Yona 1:1, 2; 3:10; 4:9-11) Pambuyo pake, Yesu anagwiritsa ntchito chitsanzo chimenechi pophunzitsa anthu zokhudza chilungamo ndi chifundo cha Yehova. Kodi anthu a ku Nineve ‘adzauka pa chiweruzo’ chiti? Yesu anaphunzitsa kuti anthu ena “adzauka kuti aweruzidwe.” (Yoh. 5:29) Iye ankanena za Ulamuliro [Wake] wa Zaka 1,000, pomwe anthu ‘olungama ndi osalungama omwe adzaukitsidwe.’ (Mac. 24:15) Kwa anthu osalungama, kumeneku kudzakhala ‘kuuka kuti aweruzidwe.’ Izi zikutanthauza kuti Yehova ndi Yesu azidzaona ngati anthuwo akumvera komanso kutsatira zimene adzaphunzitsidwe. Mwachitsanzo, ngati anthu ena a ku Nineve adzakane kulambira Yehova, adzaweruzidwa kuti asakhalenso ndi moyo. (Yes. 65:20) Koma anthu onse amene adzasankhe kulambira Yehova mokhulupirika, adzaweruzidwa kuti akhale ndi moyo mpaka kalekale.—Dan. 12:2. w24.05 5 ¶13-14
Lachisanu, June 5
Mwana wa munthu anabwera kudzafunafuna ndiponso kudzapulumutsa anthu osochera.—Luka 19:10.
Yesu anasonyeza bwino kuti Atate wake ndi wachifundo. (Yoh. 14:9) Zimene iye ankalankhula komanso kuchita zinasonyeza kuti Yehova, yemwe ndi wokoma mtima, amakonda anthu ndipo amafuna kuwathandiza kuti azimumvera komanso kumutumikira ngakhale kuti ndi ochimwa. Yesu amafuna kuti anthu ochimwa alape n’kuyamba kumutsatira. (Luka 5:27, 28) Yesu ankadziwa kuti adzapereka moyo wake monga nsembe. Mobwerezabwereza iye anauza otsatira ake kuti adzaperekedwa m’manja mwa adani komanso kupachikidwa pamtengo wozunzikirapo. (Mat. 17:22; 20:18, 19) Iye ankadziwa kuti nsembe yake idzachotsa machimo a dziko. Yesu anaphunzitsanso kuti akadzapereka moyo wake, ‘adzakokera anthu osiyanasiyana’ kwa iye. (Yoh. 12:32) Anthu ochimwa angasangalatse Yehova ngati amavomereza Yesu kukhala Mbuye wawo komanso kutengera chitsanzo chake. Iwo akamachita zimenezi pamapeto pake ‘adzamasulidwa ku uchimo.’ (Aroma 6:14, 18, 22; Yoh. 8:32) Choncho mofunitsitsa komanso molimba mtima, Yesu analolera kufa imfa yowawa kuti atipulumutse.—Yoh. 10:17, 18. w24.08 5 ¶11-12
Loweruka, June 6
Choyamba uthenga wabwino ukuyenera kulalikidwa kwa anthu amitundu yonse.—Maliko 13:10.
Taganizirani mmene munamvera mutamva koyamba choonadi cha m’Mawu a Mulungu. Munaphunzira kuti Atate wanu wakumwamba amakukondani, amafuna kuti mukhale m’banja lake la anthu omwe amamulambira, adzathetsa mavuto ndi zopweteka zonse, mukhoza kukhala ndi chiyembekezo chodzaonananso ndi okondedwa anu omwe anamwalira ndi zinanso zambiri. (Maliko 10:29, 30; Yoh. 5:28, 29; Aroma 8:38, 39; Chiv. 21:3, 4) Mfundo za choonadi zomwe munaphunzirazi zinakufikani pamtima. (Luka 24:32) Munkakonda kwambiri zimene munkaphunzirazo moti munkafunitsitsa kuuza aliyense. (Yerekezerani ndi Yeremiya 20:9.) Kunena zoona, tikamakonda mfundo za m’Baibulo ndi mtima wonse, timafunitsitsa kuuza aliyense zomwe taphunzira. (Luka 6:45) Timamva ngati ophunzira a Yesu, omwe anati: “Sitingasiye kulankhula za zinthu zimene tinaziona ndi kuzimva.” (Mac. 4:20) Timakonda kwambiri choonadi moti timafunitsitsa kuuza ena za choonadicho mmene tingathere. w24.05 15 ¶5; 16 ¶7