Lachinayi, June 1
Panafika mkazi wamasiye wosauka ndipo anaponyamo timakobidi tiwiri tating’ono.—Maliko 12:42.
Mayiyu ndi wosauka kwambiri moti amavutika kupeza zinthu zofunika pa moyo. Komabe iye akupita pomwe pali choponyamo zopereka ndipo akuponya timakobidi tiwiri, tomwe mwina sitinamveke phokoso n’komwe. Yesu wadziwa kuti mayiyu waponya timalepitoni tiwiri, tomwe tinali timakobidi tochepa mphamvu kwambiri pa nthawiyo. Ndalamayi inali yosakwana kugula ngakhale mpheta imodzi, yomwe inali m’gulu la mbalame zotchipa kwambiri zimene anthu ankadya. Yesu wachita chidwi kwambiri ndi mayi wamasiyeyu. Choncho akuitana ophunzira ake n’kuwauza kuti: “Mkazi wamasiye wosaukayu waponya zochuluka kuposa onse.” Kenako akunena kuti: “Onsewo [makamaka anthu olemera] aponya zimene atapa pa zochuluka zimene ali nazo, koma mayiyu, mu umphawi wake, waponya zonse zimene anali nazo, inde zonse zochirikizira moyo wake.” (Maliko 12:43, 44) Popereka ndalama zonse zomwe anali nazo patsikulo, mayi wamasiyeyo ankakhulupirira kwambiri kuti Yehova amusamalira.—Sal. 26:3. w21.04 6 ¶17-18
Lachisanu, June 2
Taonani tsopano! Mwadzaza Yerusalemu yense ndi chiphunzitso chanuchi.—Mac. 5:28.
Yesu ali padziko lapansili, ankaona moyenera utumiki wake ndipo amafunanso otsatira ake aziona moyenera utumiki wawo. (Yoh. 4:35, 36) Ophunzira ake ankachita khama kugwira ntchito yolalikira pamene iye anali nawo limodzi. (Luka 10:1, 5-11, 17) Koma Yesu atagwidwa komanso kuphedwa, ophunzirawo kwa kanthawi kochepa anasiya kulalikira. (Yoh. 16:32) Ndiyeno ataukitsidwa iye analimbikitsa ophunzirawo kuti ayambirenso kugwira ntchito yolalikira mwakhama. Ndipo Yesu atakwera kumwamba iwo analalikira mwakhama kwambiri moti adani awo anafika podandaula monga taonera mulemba laleroli. Yesu ankatsogolera ntchito ya Akhristu oyambirira ndipo Yehova anawadalitsa moti anthu ambiri anakhala okhulupirira. Mwachitsanzo, pa Pentekosite mu 33 C.E., anthu pafupifupi 3,000 anabatizidwa. (Mac. 2:41) Ndipo chiwerengero cha ophunzira chinapitiriza kukula kwambiri. (Mac. 6:7) Komabe Yesu ananeneratu kuti ntchito yolalikira idzawonjezeka kwambiri m’masiku otsiriza.—Yoh. 14:12; Mac. 1:8. w21.05 14 ¶1-2
Loweruka, June 3
Wodala amene sapeza chokhumudwitsa mwa ine.—Mat. 11:6.
Kodi mukukumbukira mmene munamvera mutazindikira kuti mwapeza choonadi? Munkaona ngati aliyense avomereza zimene mwayamba kukhulupirirazo. Simunkakayikira kuti uthenga wa m’Baibulo ungawathandize kukhala ndi moyo wosangalala panopa komanso kuyembekezera zinthu zabwino m’tsogolo. (Sal. 119:105) Choncho ndi mtima wonse munayamba kuuza anzanu komanso achibale anu mfundo zomwe munkaphunzira. Koma kodi chinachitika n’chiyani? Muyenera kuti munadabwa kuona kuti ambiri anakana zimene munawauza. Sitiyenera kudabwa anthu ena akamakana uthenga umene timalalikira. Mu nthawi ya Yesu, anthu ambiri anamukana ngakhale kuti ankachita zozizwitsa posonyeza kuti anatumidwa ndi Mulungu. Mwachitsanzo, Yesu anaukitsa Lazaro, chomwe chinali chozizwitsa chimene ngakhale anthu amene ankamutsutsawo sakanachikana. Ngakhale zinali choncho, atsogoleri a Chiyuda sanakhulupirire kuti Yesu ndi Mesiya ndipo anayamba kufuna kumupha limodzi ndi Lazaro.—Yoh. 11:47, 48, 53; 12:9-11. w21.05 2 ¶1-2