Lachisanu, March 28
Pitirizani kuyenda ngati ana a kuwala.—Aef. 5:8.
Akhristu a ku Efeso anali ataona kuwala kwa choonadi cha m’Malemba. (Sal. 119:105) Anali atasiya miyambo ya chipembedzo chabodza komanso makhalidwe oipa. Iwo anayamba kutsanzira Mulungu ndipo ankachita zonse zimene angathe kuti azimulambira komanso kumusangalatsa. (Aef. 5:1) Ifenso tisanaphunzire choonadi tinali mumdima pa nkhani ya kulambira komanso makhalidwe. Ena ankachita maholide a chipembedzo chabodza pomwe ena anali achiwerewere. Koma titaphunzira mfundo za Yehova pa nkhani ya zoyenera ndi zolakwika, tinasintha. Tinayamba kusintha moyo wathu kuti ugwirizane ndi mfundo zake zolungama ndipo tsopano tikupeza madalitso ambiri. (Yes. 48:17) Komabe panopa pali mavuto amene tikukumana nawo. Tiyenera kutalikirana ndi mdima womwe tinausiya n’kupitiriza “kuyenda ngati ana a kuwala.” w24.03 21 ¶6-7
Loweruka, March 29
Mulimonse mmene tapitira patsogolo, tiyeni tipitirize kupita patsogolo pochita zomwe tikuchitazo.—Afil. 3:16.
Mwina mungamaone kuti simunakonzeke kuti mudzipereke komanso kubatizidwa. N’kuthekanso kuti mukufunika kusintha zinthu zina kuti muzitsatira mfundo za Yehova. Kapenanso mukufunika nthawi yambiri kuti mulimbitse chikhulupiriro chanu. (Akol. 2:6, 7) Sikuti ophunzira onse amapita patsogolo mofanana ndiponso ana samakhala okonzeka kudzipereka komanso kubatizidwa pa msinkhu wofanana. Muziyesa kuona mmene mukupitira patsogolo mogwirizana ndi zomwe mungakwanitse ndipo musamadziyerekezere ndi munthu wina. (Agal. 6:4, 5) Ngakhale mutaona kuti simunakonzeke kudzipereka kwa Yehova, muzipitirizabe kukhala ndi cholinga chimenechi. Muzimupempha kuti akuthandizeni kukonza zomwe mukufunika kusintha. (Afil. 2:13) Dziwani kuti iye adzamva pemphero lanu ndipo adzakuthandizani.—1 Yoh. 5:14. w24.03 5 ¶9-10
Lamlungu, March 30
Amuna, pitirizani kukhala ndi akazi anu mowadziwa bwino.—1 Pet. 3:7.
Pa nthawi ina, Sara anakhumudwa kwambiri mpaka ankaimba mlandu Abulahamu kuti ndi amene anachititsa vuto limene anakumana nalo. Abulahamu ankadziwa kuti Sara anali mkazi wogonjera komanso ankamuthandiza kwambiri. Iye anamumvetsera ndipo anayesetsa kuthetsa vutolo. (Gen. 16:5, 6) Ndiye kodi tikuphunzirapo chiyani? Amuna, muli ndi udindo wosankha zochita pa nkhani zokhudza banja lanu. (1 Akor. 11:3) Komabe, mungasonyeze chikondi ngati mutamvetsera maganizo a mkazi wanu musanasankhe zochita, makamaka pa nkhani zimene zingamukhudze. (1 Akor. 13:4, 5) Pa nthawi ina, Abulahamu ankafuna kuchereza alendo omwe anafika kunyumba kwawo mwadzidzidzi. Iye anapempha Sara kuti asiye kaye zomwe ankachita, n’kukonza makeke ambiri. (Gen. 18:6) Sara anachitapo kanthu mwamsanga pochita zimene Abulahamu anamupempha. Akazi, mungatsanzire Sara pogwirizana ndi zimene amuna anu asankha. Mukamachita zimenezi, mumalimbitsa banja lanu.—1 Pet. 3:5, 6. w23.05 24-25 ¶16-17