Lachitatu, January 25
Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu, ndipo ndi akuthwa kuposa lupanga lililonse lakuthwa konsekonse. . . . amathanso kuzindikira zimene munthu akuganiza komanso zolinga za mtima wake.—Aheb. 4:12.
Kuganizira mozama zimene tawerenga m’Mawu a Mulungu kungatithandize kukhala ndi maganizo oyenera pa mavuto amene takumana nawo. Tiyeni tione mmene Baibulo linathandizira mlongo wina wamasiye yemwe anali ndi chisoni chachikulu. Mkulu wina anamuuza kuti angapeze mfundo zothandiza ngati atawerenga buku la Yobu. Atangoyamba kuwerenga bukuli, mlongoyu ankaona kuti Yobu anali ndi maganizo olakwika ndipo mumtima mwake anayamba kumudzudzula kuti: “Yobu, amenewotu si maganizo abwino.” Koma kenako anazindikira kuti nayenso anali ndi maganizo olakwika ngati Yobu. Zimenezi zinamuthandiza kuti asinthe n’kuyamba kuona zinthu moyenera komanso zinamupatsa mphamvu kuti athe kupirira ululu umene ankamva chifukwa cha imfa ya mwamuna wake. Njira ina imene Yehova amatipatsira mphamvu ndi kudzera mwa olambira anzathu. Paulo analemba kuti ankalakalaka atakumana ndi abale ndi alongo n’cholinga choti ‘alimbikitsane.’—Aroma 1:11, 12. w21.05 22 ¶10-11; 24 ¶12
Lachinayi, January 26
Uzichitira Yehova Mulungu wako chikondwerero chimenecho masiku 7 pamalo amene Yehova adzasankhe.—Deut. 16:15.
Aisiraeli anauzidwa kuti: “Mwamuna aliyense pakati panu azikaonekera katatu pa chaka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, pamalo amene Mulungu adzasankhe.” (Deut. 16:16) Iwo ankafunika kusiya nyumba ndi mbewu zawo popanda woziyang’anira. Yehova anawalonjeza kuti: “Palibe aliyense adzasirira dziko lanu pamene mwachoka kukaona nkhope ya Yehova Mulungu wanu.” (Eks. 34:24) Popeza kuti ankakhulupirira kwambiri Yehova, Aisiraeli oopa Mulunguwa ankapezeka pa zikondwererozi chaka chilichonse. Zimenezi zinkachititsa kuti azidalitsidwa kwambiri. Mwachitsanzo, ankamvetsa bwino Chilamulo cha Mulungu, kuganizira ubwino wake ndiponso ankalimbikitsidwa akasonkhana ndi olambira anzawo. Ifenso timapindula kwambiri ndi zinthu zimenezi tikamayesetsa kuti tikapezeke pamisonkhano. Komanso taganizirani mmene Yehova amasangalalira tikafika pamisonkhano titakonzekera kupereka ndemanga zachidule komanso zolimbikitsa. w22.03 22 ¶9
Lachisanu, January 27
Amatha kuthandiza anthu amene akuyesedwa.—Aheb. 2:18.
Yehova ankakonzekeretsa Yesu kuti adzakwaniritse udindo wake wam’tsogolo monga Mkulu wa Ansembe. Yesu anaona mmene zimakhalira zovuta kumvera Mulungu ukakumana ndi mayesero aakulu. Iye anapanikizika kwambiri mpaka anafika popempha Yehova kuti amuthandize, ‘akufuula komanso akugwetsa misozi.’ Popeza kuti anavutikapo kwambiri chonchi, Yesu amamvetsa mmene timamvera ndipo “amatha kuthandiza anthu amene akuyesedwa.” Timayamikira kwambiri kuti Yehova anatipatsa mkulu wa ansembe wachifundo, yemwe ‘amatimvera chisoni pa zofooka zathu.’ (Aheb. 2:17; 4:14-16; 5:7-10) Yehova analolera kuti Yesu avutike kwambiri chifukwa ankafuna kupereka yankho pa funso lofunika kwambiri, lakuti: Kodi anthu angakhalebe okhulupirika kwa Yehova ngakhale atakumana ndi mayesero aakulu? Satana amatsutsa zimenezi. Iye amanena kuti anthu amatumikira Mulungu ndi zolinga zadyera komanso kuti sakonda Yehova. (Yobu 1:9-11; 2:4, 5) Yesu anakhalabe wokhulupirika ndipo anasonyeza kuti Satana ndi wabodza. w21.04 16-17 ¶7-8