-
Madzi Alisesa DzikoKumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
-
-
Mphunzitsi Wamkuruyo anadziwa kuti chimenechi chinali chitachitika ku dziko lonse lapansi la anthu nthawi ina kalelo. Iye anati: ‘Anthu amenewo analinkudya. Iwo analinkumwa. Iwo analinkumakwatirana.’ Sikuli kolakwa kudya ndi kumwa kapena kukwatira. Koma iwo anali otanganitsidwa kwambiri kumazichita zinthu zimenezo chakuti iwo sanakhale ndi nthawi ya kumumvetsera Mulungu. Chimenecho chinali choipa.
-
-
Madzi Alisesa DzikoKumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
-
-
Kodi nchiani chimene chinawachitikira anthu amenewo?—Yesu anati: “Iwo sanadziwe kufikira chigumula chinadza nichiwasesa iwo onse.” Yesu anali kumalankhula za anthu amene anafa m’masiku a Nowa. Pa nthawi imeneyo madzi a chigumula analikuta dziko lonse lapansi.—Mateyu 24:37-39, NW.
-
-
Madzi Alisesa DzikoKumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
-
-
Kodi Yehova anawapatsa anthu ena mwai wa kulowa m’chingalawacho ndi kupulumutsidwa?—Inde, iye anawapatsa. Yehova anamuuza Nowa kulalikira. Chotero mkati mwa zaka zonsezo zimene chingalawacho chinali kumamamgidwa, Nowa anawachenjeza anthuwo ponena za chigumula chinalinkudzacho.
Kodi ali onse a iwo anamvetsera?—Banja la Nowa lokha linamvetsera. Ena onse anali ongotanganitsidwa kwambiri kumachita zinthu zina. Iwo sanaganize kuti iwo anali oipa kwambiri, ndipo iwo sanakhale ndi nthawi ya kumvetsera.
-