16 Koma Mulungu wa Yakobo+ sali ngati mafanowa. Iye ndi amene anapanga china chilichonse.+ Isiraeli ndiye ndodo ya cholowa chake.+ Dzina la Mulunguyo ndi Yehova wa makamu.+
14 Weta anthu ako ndi ndodo yako.+ Weta gulu la nkhosa zomwe ndi cholowa chako, zimene zinali kukhala zokhazokha m’nkhalango pakati pa mitengo ya zipatso.+ Uzilole kuti zikadyere ku Basana ndi ku Giliyadi+ ngati mmene zinali kuchitira masiku akale.+