1 Akorinto
15 Tsopano abale, ndikukuuzani uthenga wabwino+ umene ndinaulengeza kwa inu,+ umenenso munaulandira, ndiponso umene mwakhazikikamo.+ 2 Mukupulumutsidwa+ ndi uthenga wabwino umenewo ngati mwaugwiritsitsa. Popanda kutero, ndiye kuti munakhala okhulupirira pachabe,+ malinga ndi mawu amene ndinakuuzani polengeza uthengawo kwa inu.
3 Mwa zinthu zofunika kwambiri zimene ndinakupatsirani zija, zimenenso ineyo ndinalandira,+ panali zonena kuti, Khristu anafera machimo athu, malinga ndi Malemba.+ 4 Ndiponso kuti anaikidwa m’manda,+ kenako anaukitsidwa+ tsiku lachitatu,+ mogwirizana ndi Malemba.+ 5 Panalinso zoti anaonekera kwa Kefa,+ kenako kwa atumwi 12+ aja. 6 Ndiyeno anaonekeranso kwa abale oposa 500 pa nthawi imodzi, ndipo ambiri a iwo akali ndi moyo mpaka lero,+ koma ena anagona mu imfa. 7 Kenako anaonekera kwa Yakobo,+ kenakonso kwa atumwi onse.+ 8 Koma pomalizira pake anaonekera kwa ine,+ ngati khanda lobadwa masiku asanakwane.
9 Ineyo ndine wamng’ono kwambiri+ mwa atumwi onse, ndipo si ine woyenera kutchedwa mtumwi, chifukwa ndinazunza+ mpingo wa Mulungu. 10 Koma mwa kukoma mtima kwakukulu+ kwa Mulungu, ndili monga ndililimu. Ndipo kukoma mtima kwake kwakukulu kumene anandisonyeza sikunapite pachabe,+ koma ndinagwira ntchito molimbika kuposa atumwi ena onse.+ Ngakhale zili choncho, si mwa ine ndekha ayi, koma kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu kumene kuli nane.+ 11 Komabe, kaya ndi ineyo kapena iwowo, zimene tikulalikira ndi zomwezo, zimenenso mwazikhulupirirazo.+
12 Tsopano ngati timalalikira kuti Khristu anaukitsidwa kwa akufa,+ bwanji ena mwa inu akunena kuti akufa sadzaukitsidwa?+ 13 Chifukwa ngati akufa sadzauka, ndiye kuti Khristu nayenso sanauke.+ 14 Koma ngati Khristu sanauke, kulalikira kwathu n’kopanda pake, ndipo chikhulupiriro chathu n’chopanda pake.+ 15 Ndiponso, ndiye kuti ifenso takhala mboni zonama za Mulungu,+ chifukwa tachita umboni+ wonamizira Mulungu kuti anaukitsa Khristu+ pamene sanamuukitse, ngati akufa sadzaukadi.+ 16 Pakuti ngati akufa sadzauka, Khristunso sanauke. 17 Ndipo ngati Khristu sanauke, chikhulupiriro chanu chilibe ntchito ndipo mukadali m’machimo anu.+ 18 Ndiye kutinso anthu amene anagona mu imfa mwa Khristu,+ kutha kwawo kunali komweko.+ 19 Ngati tayembekezera Khristu+ m’moyo uno wokha, ndiye kuti ndife omvetsa chisoni kuposa anthu ena onse.
20 Komabe, Khristu anaukitsidwa kwa akufa,+ n’kukhala chipatso choyambirira+ cha amene akugona mu imfa.+ 21 Popeza imfa+ inafika kudzera mwa munthu mmodzi, kuuka+ kwa akufa kunafikanso kudzera mwa munthu mmodzi. 22 Pakuti monga mwa Adamu onse akufa,+ momwemonso mwa Khristu onse adzapatsidwa+ moyo. 23 Koma aliyense pamalo pake: Choyamba Khristu, amene ndi chipatso choyambirira,+ kenako ake a Khristu pa nthawi ya kukhalapo*+ kwake. 24 Ndiyeno pa mapeto pake, adzapereka ufumu kwa Mulungu wake ndi Atate wake, atathetsa maboma onse, ulamuliro wonse, ndi mphamvu zonse.+ 25 Pakuti ayenera kulamulira monga mfumu kufikira Mulungu ataika adani onse pansi pa mapazi+ ake. 26 Imfa nayonso, monga mdani womalizira, idzawonongedwa.+ 27 Pakuti Mulungu “anaika zinthu zonse pansi pa mapazi ake.”+ Koma pamene akunena kuti ‘waika zinthu zonse pansi pake,’+ n’zodziwikiratu kuti sakuphatikizapo amene anaika zinthu zonsezo pansi pa iye.+ 28 Koma zinthu zonse zikadzakhala pansi pake,+ Mwanayonso adzadziika pansi pa amene+ anaika zinthu zonse pansi pake, kuti Mulungu akhale zinthu zonse kwa aliyense.+
29 Apo ayi, kodi amene akubatizidwa kuti akhale akufa adzatani?+ Ngati akufa sadzauka,+ n’chifukwa chiyani anthuwo akubatizidwa+ kuti akhale akufa? 30 Kodi ifeyo tikuikiranji moyo wathu pachiswe nthawi zonse?+ 31 Tsiku ndi tsiku ndimakhala pa ngozi yoti ndikhoza kufa.+ Ndikukutsimikizirani zimenezi ndili wokondwera nanu,+ abale, kukondwera kumene ndili nako mwa Khristu Yesu Ambuye wathu. 32 Ngati ndinamenyana ndi zilombo ku Efeso+ monga ena anachitira, ndinapindulapo chiyani? Ngati akufa sadzauka, “tiyeni tidye ndi kumwa, pakuti mawa tifa.”+ 33 Musasocheretsedwe. Kugwirizana ndi anthu oipa kumawononga makhalidwe abwino.+ 34 Dzukani ku tulo tanu+ kuti mukhale olungama ndipo musamachite tchimo, pakuti ena sadziwa Mulungu.+ Ndikulankhula zimenezi kuti muchite manyazi.+
35 Ngakhale zili choncho, wina anganene kuti: “Kodi akufa adzaukitsidwa motani? Inde, kodi iwo adzauka ndi thupi lotani?”+ 36 Wopusa iwe! Chimene wabzala sichikhala ndi moyo pokhapokha chitafa kaye.+ 37 Ndipo chimene wafesa si mmera umene umakulawo, koma mbewu chabe,+ kaya ya tirigu kapena ina iliyonse. 38 Koma Mulungu amaipatsa thupi+ monga mwa kufuna kwake,+ ndipo mbewu iliyonse amaipatsa thupi lake. 39 Mnofu sukhala wa mtundu umodzi, koma pali mnofu wa munthu, ndipo pali wa nyama, palinso wa mbalame, ndi winanso wa nsomba.+ 40 Palinso matupi akumwamba,+ ndi matupi+ apadziko lapansi, koma ulemerero+ wa matupi akumwamba ndi wina, ndipo ulemerero wa matupi apadziko lapansi ndi winanso. 41 Ulemerero wa dzuwa+ ndi wosiyana ndi ulemerero wa mwezi,+ ndipo ulemerero wa nyenyezi ndi winanso. Ngakhale ulemerero wa nyenyezi+ ina, umasiyana ndi ulemerero wa inzake.
42 Ndi mmenenso zilili ndi kuuka kwa akufa.+ Thupi limafesedwa lili lokhoza kuwonongeka, limaukitsidwa losakhoza kuwonongeka.+ 43 Limafesedwa lonyozeka,+ limaukitsidwa mu ulemerero.+ Limafesedwa lofooka,+ limaukitsidwa mu mphamvu.+ 44 Limafesedwa thupi lanyama,+ limaukitsidwa thupi lauzimu.+ Ngati pali thupi lanyama, palinso lauzimu. 45 Zinachita kulembedwa kuti: “Munthu woyambirira, Adamu, anakhala munthu wamoyo.”+ Adamu womalizira anakhala mzimu+ wopatsa moyo.+ 46 Ngakhale zili choncho, choyambacho si chauzimu ayi koma chamnofu. Kenako panabwera chauzimu.+ 47 Munthu woyambayo anachokera padziko lapansi ndipo anapangidwa ndi fumbi.+ Wachiwiriyo anachokera kumwamba.+ 48 Mmene wopangidwa ndi fumbiyo alili,+ ndi mmenenso opangidwa ndi fumbiwo alili. Ndipo mmene wakumwambayo alili,+ ndi mmenenso akumwambawo alili.+ 49 Ndiponso, monga tilili m’chifaniziro+ cha wopangidwa ndi fumbi uja, tidzakhalanso m’chifaniziro+ cha wakumwambayo.
50 Koma abale, ndikunenetsa kuti mnofu ndi magazi sizingalowe ufumu wa Mulungu.+ Komanso chowonongeka sichingalandire kusawonongeka.+ 51 Tamverani! Ndikukuuzani chinsinsi chopatulika: Si tonse amene tidzagona mu imfa, koma tonse tidzasandulika,+ 52 m’kamphindi, m’kuphethira kwa diso, pa kulira kwa lipenga lomaliza. Pakuti lipengalo+ lidzalira, ndipo akufa adzaukitsidwa osakhoza kuwonongeka, ndipo tidzasandulika. 53 Pakuti chokhoza kuwonongekachi chidzavala kusawonongeka,+ ndipo chokhoza kufachi+ chidzavala kusafa. 54 Koma chokhoza kuwonongekachi chikadzavala kusawonongeka, ndipo chokhoza kufachi chikadzavala kusafa, pamenepo adzakwaniritsidwa mawu amene analembedwa kuti: “Imfa+ yamezedwa kwamuyaya.”+ 55 “Imfa iwe, kupambana kwako kuli kuti? Imfawe, mphamvu yako ili kuti?”+ 56 Mphamvu+ imene imabala imfa ndiyo uchimo, koma mphamvu ya uchimo ndi Chilamulo.+ 57 Koma Mulungu ayamikike, pakuti amatithandiza kuti tipambane kudzera mwa Ambuye wathu Yesu Khristu.+
58 Choncho abale anga okondedwa, khalani olimba,+ osasunthika, okhala ndi zochita zambiri nthawi zonse mu ntchito ya Ambuye,+ podziwa kuti zonse zimene mukuchita mu ntchito ya Ambuye sizidzapita pachabe.+